Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Miyambo 21:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Nsembe ya anthu oipa ndi yonyansa.+ Ndiye kuli bwanji munthu akaiperekera limodzi ndi makhalidwe otayirira?+

  • Yesaya 1:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Yehova wanena kuti: “Kodi nsembe zanu zambirimbirizo zili ndi phindu lanji kwa ine? Nsembe zopsereza zathunthu+ za nkhosa zamphongo+ ndiponso mafuta a nyama zodyetsedwa bwino zandikwana.+ Ine sindikusangalalanso+ ndi magazi+ a ana a ng’ombe amphongo, ana a nkhosa amphongo ndiponso a mbuzi zamphongo.+

  • Yesaya 66:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 “Munthu amene akupha ng’ombe yamphongo ali ngati wopha munthu.+ Amene akupereka nsembe ya nkhosa ali ngati wothyola khosi la galu.+ Wopereka mphatso ali ngati wopereka magazi a nkhumba.+ Wopereka lubani wachikumbutso+ ali ngati wopereka dalitso pogwiritsa ntchito mawu onenerera zamatsenga.+ Anthuwo asankha njira zawozawo, ndipo amasangalala ndi zinthu zawo zonyansa.+

  • Yeremiya 6:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 “N’chifukwa chiyani mukundibweretsera lubani* wochokera ku Sheba+ ndi mabango onunkhira ochokera kudziko lakutali? Zimenezi zili ndi ntchito yanji kwa ine? Nsembe zanu zopsereza zathunthu sizikundisangalatsa,+ ndipo nsembe zina zonse zimene mukupereka sizikundikondweretsa.”+

  • Mateyu 23:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu! Chifukwa mumapereka chakhumi+ cha timbewu ta minti, dilili, ndi chitowe, koma mumanyalanyaza zinthu zofunika za m’Chilamulo, monga chilungamo,+ chifundo+ ndi kukhulupirika.+ Kupereka zinthu zimenezi n’kofunikadi, koma osanyalanyaza zinthu zinazo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena