41 Choncho, Esau anasunga chidani kwa Yakobo mumtima mwake.+ Anamuda chifukwa cha madalitso amene bambo ake anamupatsa. Iye anapitiriza kunena mumtima mwake+ kuti: “Masiku olira maliro a bambo anga ali pafupi.+ Pambuyo pake, ndidzamupha m’bale wanga Yakobo.”+