Deuteronomo 6:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Uziopa Yehova Mulungu wako+ ndi kum’tumikira,+ ndipo uzilumbira pa dzina lake.+ Rute 1:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Kumene inu mudzafere inenso ndidzafera komweko,+ ndipo ndidzaikidwanso komweko. Yehova andilange kwambiri+ ngati chinachake kupatulapo imfa chingandilekanitse ndi inu.” 1 Samueli 3:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Ndiyeno Eli anamuuza kuti: “Kodi Mulungu wakuuza chiyani? Chonde usandibisire ayi.+ Mulungu akulange ndi kuwonjezerapo,+ ukandibisira ngakhale mawu amodzi pa mawu onse amene iye wakuuza.” 2 Samueli 19:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Amasa mumuuze kuti,+ ‘Kodi iwe sindiwe fupa langa ndi mnofu wanga? Mulungu andilange mowirikiza+ ngati sudzakhala mtsogoleri wa gulu langa lankhondo nthawi zonse m’malo mwa Yowabu.’”+
17 Kumene inu mudzafere inenso ndidzafera komweko,+ ndipo ndidzaikidwanso komweko. Yehova andilange kwambiri+ ngati chinachake kupatulapo imfa chingandilekanitse ndi inu.”
17 Ndiyeno Eli anamuuza kuti: “Kodi Mulungu wakuuza chiyani? Chonde usandibisire ayi.+ Mulungu akulange ndi kuwonjezerapo,+ ukandibisira ngakhale mawu amodzi pa mawu onse amene iye wakuuza.”
13 Amasa mumuuze kuti,+ ‘Kodi iwe sindiwe fupa langa ndi mnofu wanga? Mulungu andilange mowirikiza+ ngati sudzakhala mtsogoleri wa gulu langa lankhondo nthawi zonse m’malo mwa Yowabu.’”+