26 momwemonso sindidzakana mbewu ya Yakobo ndi mbewu ya Davide mtumiki wanga,+ kuti pakati pa mbewu yake nditengepo olamulira mbewu ya Abulahamu, Isaki ndi Yakobo. Pakuti ndidzasonkhanitsa onse amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina+ ndipo ndidzawamvera chisoni.’”+