7 Koma ndidzachitira chifundo nyumba ya Yuda,+ ndipo Ine Yehova Mulungu wawo, ndidzawapulumutsa.+ Sindidzawapulumutsa ndi uta, lupanga, nkhondo, mahatchi* kapena ndi amuna okwera pamahatchi ayi.”+
6 Ndidzachititsa nyumba ya Yuda kukhala yapamwamba ndipo nyumba ya Yosefe ndidzaipulumutsa.+ Ndidzawachitira chifundo ndipo ndidzawapatsa malo okhala.+ Iwo adzakhala ngati sanakanidwepo chiyambire.+ Pakuti ine ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.+