Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 14:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Pakuti Yehova adzachitira chifundo Yakobo+ ndipo adzasankhanso Isiraeli.+ Iye adzawapatsa mpumulo m’dziko lawo.+ Alendo adzakhala nawo limodzi ndipo adzadziphatika kunyumba ya Yakobo.+

  • Yeremiya 31:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 “Kodi Efuraimu si mwana wanga wamtengo wapatali, kapena mwana wanga wokondedwa?+ Pamlingo umene ndalankhula zomulanga, ndidzakumbukira kumuchitira zabwino pamlingo womwewo.+ N’chifukwa chake m’mimba mwanga mukubwadamuka chifukwa cha iye.+ Mosalephera ndidzamumvera chisoni,”+ watero Yehova.

  • Hoseya 1:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Koma ndidzachitira chifundo nyumba ya Yuda,+ ndipo Ine Yehova Mulungu wawo, ndidzawapulumutsa.+ Sindidzawapulumutsa ndi uta, lupanga, nkhondo, mahatchi* kapena ndi amuna okwera pamahatchi ayi.”+

  • Mika 7:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Inu mudzatichitiranso chifundo+ ndipo mudzapondaponda zolakwa zathu.+ Machimo athu onse mudzawaponya pakati pa nyanja yozama.+

  • Zekariya 10:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ndidzachititsa nyumba ya Yuda kukhala yapamwamba ndipo nyumba ya Yosefe ndidzaipulumutsa.+ Ndidzawachitira chifundo ndipo ndidzawapatsa malo okhala.+ Iwo adzakhala ngati sanakanidwepo chiyambire.+ Pakuti ine ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena