12 Zeba ndi Zalimuna atathawa, iye mosazengereza anawathamangitsa mpaka kuwagwira mafumu a Midiyaniwa.+ Atatero, anachititsa gulu lawo lonse kunjenjemera ndi mantha.
28 Choncho, Amidiyani+ anagonjetsedwa ndi ana a Isiraeli, ndipo Amidiyani sanakwezenso mutu wawo. Zitatero, dziko linakhala pa mtendere zaka 40 m’masiku a Gidiyoni.+