Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mbiri 32:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Tsopano Yehova anatumiza mngelo+ yemwe anapha mwamuna aliyense wamphamvu ndi wolimba mtima,+ komanso mtsogoleri ndi mkulu wa asilikali aliyense mumsasa wa mfumu ya Asuri,+ moti mfumuyo inabwerera kwawo mwamanyazi. Kenako inalowa m’kachisi wa mulungu wake ndipo ili mmenemo, ena mwa ana ake anaipha ndi lupanga.+

  • Yesaya 30:32
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Ulendo uliwonse umene Yehova adzakwapule Asuri ndi ndodo yake, kudzamveka kulira kwa maseche ndi azeze.+ Pomenyana nawo, iye azidzazunguza zida zake uku ndi uku.+

  • Yesaya 37:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 Ndiyeno mngelo+ wa Yehova anapita kumsasa wa Asuri n’kukapha asilikali 185,000.+ Anthu podzuka m’mawa, anangoona kuti onse aja ndi mitembo yokhayokha.+

  • Mika 7:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Mdani wanga adzaona zimenezi, ndipo amene anali kunena kuti: “Yehova Mulungu wako ali kuti?”+ adzachita manyazi.+ Maso anga adzamuyang’ana.+ Iye adzakhala malo opondedwapondedwa ngati matope a mumsewu.+

  • Nahumu 3:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Aliyense wokuona adzakuthawa+ ndipo adzanena kuti, ‘Nineve wasakazidwa! Ndani adzamuchitira chisoni?’ Kodi anthu oti akutonthoze ndiwapeza kuti?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena