Yesaya 13:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Nyama zam’tchire zokhala kumadera opanda madzi zidzagona kumeneko, ndipo nyumba za anthu amene anali kukhala kumeneko zidzadzaza ndi akadzidzi.+ Nthiwatiwa zizidzakhala kumeneko, ndipo ziwanda zooneka ngati mbuzi* zizidzadumphadumpha kumeneko.+ Yeremiya 50:39 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 39 Choncho nyama za m’madera opanda madzi, nyama zokonda kulira mokuwa ndi nthiwatiwa zidzakhala mmenemo.+ Simudzakhalanso munthu mmenemo ndipo mzindawo sudzapezekanso ku mibadwomibadwo.”+ Yeremiya 51:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 “Ine ndikuthira nkhondo iwe+ phiri lowononga,+ amene wawononga dziko lonse lapansi.+ Ndidzatambasula dzanja langa ndi kukuthira nkhondo. Ndidzakugubuduza kukuchotsa pamatanthwe ndipo ndidzakusandutsa phiri lotenthedwa ndi moto,” watero Yehova.+ Yeremiya 51:62 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 62 Ukanene kuti, ‘Inu Yehova! Inu mwanena zowononga malo ano ndi kuwafafaniza kuti pasapezekenso chilichonse chokhalamo.+ Musapezeke munthu kapena chiweto koma mzindawo ukhale bwinja mpaka kalekale.’ Chivumbulutso 18:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Iye anafuula ndi mawu amphamvu,+ akuti: “Wagwa! Babulo Wamkulu wagwa,+ ndipo wakhala malo okhala ziwanda, ndiponso obisalamo mpweya+ uliwonse wonyansa wotuluka m’kamwa, komanso obisalamo mbalame iliyonse yonyansa ndi yodedwa.+
21 Nyama zam’tchire zokhala kumadera opanda madzi zidzagona kumeneko, ndipo nyumba za anthu amene anali kukhala kumeneko zidzadzaza ndi akadzidzi.+ Nthiwatiwa zizidzakhala kumeneko, ndipo ziwanda zooneka ngati mbuzi* zizidzadumphadumpha kumeneko.+
39 Choncho nyama za m’madera opanda madzi, nyama zokonda kulira mokuwa ndi nthiwatiwa zidzakhala mmenemo.+ Simudzakhalanso munthu mmenemo ndipo mzindawo sudzapezekanso ku mibadwomibadwo.”+
25 “Ine ndikuthira nkhondo iwe+ phiri lowononga,+ amene wawononga dziko lonse lapansi.+ Ndidzatambasula dzanja langa ndi kukuthira nkhondo. Ndidzakugubuduza kukuchotsa pamatanthwe ndipo ndidzakusandutsa phiri lotenthedwa ndi moto,” watero Yehova.+
62 Ukanene kuti, ‘Inu Yehova! Inu mwanena zowononga malo ano ndi kuwafafaniza kuti pasapezekenso chilichonse chokhalamo.+ Musapezeke munthu kapena chiweto koma mzindawo ukhale bwinja mpaka kalekale.’
2 Iye anafuula ndi mawu amphamvu,+ akuti: “Wagwa! Babulo Wamkulu wagwa,+ ndipo wakhala malo okhala ziwanda, ndiponso obisalamo mpweya+ uliwonse wonyansa wotuluka m’kamwa, komanso obisalamo mbalame iliyonse yonyansa ndi yodedwa.+