Deuteronomo 28:49 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 49 “Yehova adzautsa mtundu wakutali, kumalekezero a dziko,+ mtundu umene chilankhulo chake sudzachimva.+ Mtunduwo udzakuukira monga mmene chiwombankhanga chimakhwathulira nyama yake,+ Yesaya 5:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 Iye waikira chizindikiro mtundu waukulu wakutali.+ Wauimbira likhweru kumapeto kwa dziko lapansi.+ Ndipotu mtunduwo udzachita changu n’kubwera msangamsanga.+ Yeremiya 4:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Taonani! Mdani adzabwera ngati mitambo yamvula ndipo magaleta* ake ali ngati mphepo yamkuntho.+ Mahatchi* ake ndi aliwiro kuposa ziwombankhanga.+ Tsoka ife chifukwa tafunkhidwa. Hoseya 8:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 “Ika lipenga la nyanga ya nkhosa pakamwa pako ndipo ulilize.+ Mdani akubwera ngati chiwombankhanga+ kudzaukira nyumba ya Yehova. Akubwera chifukwa Aisiraeli aphwanya pangano langa+ ndiponso aphwanya malamulo anga.+ Habakuku 1:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Mahatchi* ake ndi aliwiro kuposa akambuku* ndiponso ndi oopsa kuposa mimbulu yoyenda usiku.+ Mahatchi ake ankhondo amachita mgugu ndipo amachokera kutali. Mahatchiwo amauluka ngati chiwombankhanga chimene chikuthamangira chakudya chake.+
49 “Yehova adzautsa mtundu wakutali, kumalekezero a dziko,+ mtundu umene chilankhulo chake sudzachimva.+ Mtunduwo udzakuukira monga mmene chiwombankhanga chimakhwathulira nyama yake,+
26 Iye waikira chizindikiro mtundu waukulu wakutali.+ Wauimbira likhweru kumapeto kwa dziko lapansi.+ Ndipotu mtunduwo udzachita changu n’kubwera msangamsanga.+
13 Taonani! Mdani adzabwera ngati mitambo yamvula ndipo magaleta* ake ali ngati mphepo yamkuntho.+ Mahatchi* ake ndi aliwiro kuposa ziwombankhanga.+ Tsoka ife chifukwa tafunkhidwa.
8 “Ika lipenga la nyanga ya nkhosa pakamwa pako ndipo ulilize.+ Mdani akubwera ngati chiwombankhanga+ kudzaukira nyumba ya Yehova. Akubwera chifukwa Aisiraeli aphwanya pangano langa+ ndiponso aphwanya malamulo anga.+
8 Mahatchi* ake ndi aliwiro kuposa akambuku* ndiponso ndi oopsa kuposa mimbulu yoyenda usiku.+ Mahatchi ake ankhondo amachita mgugu ndipo amachokera kutali. Mahatchiwo amauluka ngati chiwombankhanga chimene chikuthamangira chakudya chake.+