Deuteronomo 28:65 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 65 Pakati pa mitundu imeneyo sudzakhala mwamtendere,+ ndipo sudzapeza malo oti phazi lako liponde kuti lipumulirepo. Kumeneko, Yehova adzakupatsa mtima wachinthenthe,+ adzachititsa maso ako+ khungu ndipo adzakutayitsa mtima. Yobu 17:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Chifukwa cha kuzunzika, diso langa layamba kuchita mdima.+Ziwalo zanga zonse zakhala ngati mthunzi. Salimo 6:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Maso anga achita mdima chifukwa cha chisoni changa.+Maso anga akalamba chifukwa cha anthu onse ondichitira zoipa.+ Yesaya 59:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 Tikungoyenda ndi khoma ngati anthu akhungu, ndipo tikungofufuzafufuza ngati anthu opanda maso.+ Tapunthwa masanasana ngati kuti tili mu mdima wamadzulo. Pakati pa anthu ojintcha, tikungokhala ngati anthu akufa.+ Maliro 2:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Maso anga atopa ndi kulira.+ M’mimba mwanga mukubwadamuka.+Chiwindi changa chakhuthulidwa+ pansi chifukwa cha kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,+Ndiponso chifukwa chakuti ana ndi makanda oyamwa akukomoka+ m’mabwalo a mzinda.
65 Pakati pa mitundu imeneyo sudzakhala mwamtendere,+ ndipo sudzapeza malo oti phazi lako liponde kuti lipumulirepo. Kumeneko, Yehova adzakupatsa mtima wachinthenthe,+ adzachititsa maso ako+ khungu ndipo adzakutayitsa mtima.
7 Chifukwa cha kuzunzika, diso langa layamba kuchita mdima.+Ziwalo zanga zonse zakhala ngati mthunzi.
7 Maso anga achita mdima chifukwa cha chisoni changa.+Maso anga akalamba chifukwa cha anthu onse ondichitira zoipa.+
10 Tikungoyenda ndi khoma ngati anthu akhungu, ndipo tikungofufuzafufuza ngati anthu opanda maso.+ Tapunthwa masanasana ngati kuti tili mu mdima wamadzulo. Pakati pa anthu ojintcha, tikungokhala ngati anthu akufa.+
11 Maso anga atopa ndi kulira.+ M’mimba mwanga mukubwadamuka.+Chiwindi changa chakhuthulidwa+ pansi chifukwa cha kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,+Ndiponso chifukwa chakuti ana ndi makanda oyamwa akukomoka+ m’mabwalo a mzinda.