6 M’chaka cha 9 cha Hoshiya, mfumu ya Asuri inalanda Samariya+ n’kutenga Aisiraeli kupita nawo ku Asuri.+ Mfumuyo inakaika Aisiraeliwo ku Hala+ ndi ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani,+ ndiponso m’mizinda ya Amedi.+
10 Pamapeto pa zaka zitatu, Asuriwo analanda mzindawo.+ Anaulanda m’chaka cha 6 cha Hezekiya, kutanthauza chaka cha 9 cha Hoshiya mfumu ya Isiraeli. Chotero Samariya analandidwa.+