3 Yehova anandiuza kuti: “Yambanso kukonda mkazi wokondedwa ndi mwamuna,+ mkazi amene akuchita chigololo. Ukamukonde ngati mmene Yehova akukondera ana a Isiraeli,+ ngakhale kuti iwo akutembenukira kwa milungu ina,+ imene amakonda kuipatsa nsembe za mphesa zouma zoumba pamodzi.”+