22 Atamva zimenezo, Yesu anamuuza kuti: “Pali chinthu chimodzi chimene chikusowekabe mwa iwe: Kagulitse zinthu zonse zimene uli nazo n’kugawa ndalamazo kwa anthu osauka. Ukatero udzakhala ndi chuma kumwamba, ndiyeno ubwere udzakhale wotsatira wanga.”+