10 Koma zinamukomera Yehova kuti mtumiki wake aphwanyidwe.+ Iye anamulola kuti adwale.+ Mukapereka moyo wake monga nsembe ya kupalamula,+ iye adzaona ana ake.+ Adzatalikitsa masiku ake+ ndipo ndi dzanja lake, adzakwaniritsa zokonda+ Yehova.+
23 Munthu ameneyu, monga woperekedwa mwa kufuna kwa Mulungu ndi kudziwiratu kwake zam’tsogolo,+ ndi amene inu munamukhomerera pamtengo ndi kumupha kudzera mwa anthu osamvera malamulo.+