25 Pakuti sindikufuna kuti mukhale osadziwa abale za chinsinsi chopatulika+ chimenechi, kuopera kuti mungadzione ngati ochenjera. Chinsinsi chopatulikacho n’chakuti ena mu Isiraeli aumitsa mitima yawo+ mpaka chiwerengero chonse+ cha anthu ochokera m’mitundu ina chitakwanira.+
4 Ndiyeno ndinamva chiwerengero cha amene anadindidwa chidindo. Anthu okwana 144,000,+ ochokera m’fuko lililonse+ la ana a Isiraeli,+ anadindidwa chidindo: