12 N’zoona kuti munayenera kukhala aphunzitsi+ pofika nthawi ino. Koma sizili choncho, ndipo mukufunikanso wina woti akuphunzitseni mfundo zoyambirira+ za m’mawu opatulika a Mulungu,+ kuyambira pa chiyambi. Inu mwakhala ngati munthu wofunika mkaka, osati chakudya chotafuna.+