Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 14:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Kenako wansembe azidontheza magaziwo maulendo 7 pamunthu amene akudziyeretsa ku khateyo, ndipo azigamula kuti munthuyo ndi woyera. Akatero aziulutsa mbalame yamoyo ija pabwalo.+

  • Levitiko 14:53
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 53 Kenako aziulutsa mbalame yamoyo ija pabwalo, kunja kwa mzinda. Akatero aziyeretsa nyumbayo, ndipo idzakhala yoyera.

  • Levitiko 16:21, 22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Ndipo Aroni aziika manja ake onse pamutu pa mbuziyo ndi kuvomereza zolakwa zonse za Aisiraeli ndiponso machimo awo onse. Zonsezi aziziika pamutu pa mbuzi+ ija nʼkuipereka kwa munthu amene amusankhiratu kuti akaisiye kuchipululu. 22 Mbuziyo izinyamula zolakwa zawo zonse+ pamutu pake ndipo aziitumiza kuchipululu.+

  • Yesaya 53:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Zoonadi, iye ananyamula matenda athu,+

      Ndipo anasenza zowawa zathu.+

      Koma ifeyo tinkamuona ngati munthu amene wagwidwa ndi matenda, amene walangidwa* ndi Mulungu ndiponso kuzunzidwa.

  • Aroma 15:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Chifukwa ngakhale Khristu sankachita zinthu zodzikondweretsa yekha,+ koma anachita zimene Malemba amanena kuti: “Chipongwe cha anthu amene amakunyozani chandigwera.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena