Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 8:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Tsopano inu Yehova Mulungu wa Isiraeli, mukwaniritse lonjezo limene munalonjeza mtumiki wanu Davide bambo anga lakuti, ‘Anthu a mʼbanja lako sadzasiya kukhala pampando wachifumu wa Isiraeli. Chofunika nʼchakuti ana ako asamale mayendedwe awo poyenda mokhulupirika mʼnjira zanga ngati mmene iwe wachitira.’+

  • Salimo 89:3, 4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Mulungu anati: “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga.+

      Ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti:+

       4 ‘Ndidzachititsa kuti mbadwa* zako zikhalepo mpaka kalekale,+

      Ndipo ndidzachititsa kuti ufumu* wako ukhalepo ku mibadwo yonse.’”+ (Selah)

  • Salimo 89:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Ndapeza Davide mtumiki wanga,+

      Ndipo ndamudzoza ndi mafuta anga opatulika.+

  • Salimo 89:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 Mbadwa* zake zidzakhalapo mpaka kalekale,+

      Ndipo mpando wake wachifumu udzakhala pamaso panga kwamuyaya ngati dzuwa.+

  • Yesaya 9:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Ulamuliro* wake udzafika kutali

      Ndipo mtendere sudzatha,+

      Pampando wachifumu wa Davide+ ndiponso mu ufumu wake

      Kuti iye achititse ufumuwo kukhazikika+ ndiponso kukhala wolimba

      Pogwiritsa ntchito chilungamo+ ndiponso mtima wowongoka,+

      Kuyambira panopa mpaka kalekale.

      Yehova wa magulu ankhondo akumwamba adzachita zimenezi modzipereka kwambiri.

  • Yeremiya 33:20, 21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 “Yehova wanena kuti, ‘Ngati anthu inu mungathe kuphwanya pangano langa loti kukhale masana ndi pangano langa loti kukhale usiku, kuti masana ndi usiku zisafike pa nthawi yake,+ 21 ndiye kuti inenso ndingathe kuphwanya pangano langa ndi Davide mtumiki wanga+ kuti asakhale ndi mwana woti adzalamulire monga mfumu pampando wake wachifumu wa Davide.+ Ndingachitenso chimodzimodzi ndi pangano langa ndi atumiki anga Alevi omwe ndi ansembe.+

  • Mateyu 9:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Yesu akuchokera kumeneko, amuna awiri amene anali ndi vuto losaona+ anamutsatira akufuula kuti: “Mutichitire chifundo, Mwana wa Davide.”

  • Luka 1:69
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 69 Iye watikwezera nyanga yachipulumutso*+ mʼnyumba ya mtumiki wake Davide,+

  • Machitidwe 2:30, 31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Iye anali mneneri ndipo ankadziwa kuti Mulungu anamulonjeza polumbira, kuti pampando wake wachifumu adzakhazikapo mmodzi wa mbadwa zake.+ 31 Iye anadziwiratu zamʼtsogolo ndipo ananeneratu za kuuka kwa Khristu kuti sanasiyidwe mʼManda,* komanso thupi lake silinavunde.+

  • Machitidwe 13:22, 23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Atamuchotsa ameneyu, anawapatsa Davide kuti akhale mfumu yawo.+ Iyeyu Mulungu anamuchitira umboni kuti, ‘Ndapeza Davide mwana wa Jese,+ munthu wapamtima panga.+ Ameneyu adzachita zonse zimene ndikufuna.’ 23 Mogwirizana ndi lonjezo lake, kuchokera pa mbadwa* za munthu ameneyu, Mulungu wabweretsa mpulumutsi mu Isiraeli, amene ndi Yesu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena