Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 9:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Koma Afarisi ankanena kuti: “Ameneyu amatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya wolamulira ziwanda.”+

  • Mateyu 10:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Wophunzira amangofanana ndi mphunzitsi wake ndipo kapolo amangofanana ndi mbuye wake.+ Ngati anthu atchula mwininyumba kuti Belezebule,*+ kuli bwanji ena a mʼbanja lakelo?

  • Mateyu 12:24-29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Afarisi atamva zimenezi ananena kuti: “Ameneyutu sikuti amatulutsa ziwanda ndi mphamvu zake ayi koma ndi mphamvu za Belezebule,* wolamulira ziwanda.”+ 25 Atadziwa maganizo awo, iye anawauza kuti: “Ufumu uliwonse wogawanika umatha ndipo mzinda kapena nyumba iliyonse yogawanika sikhalitsa. 26 Mofanana ndi zimenezi, ngati Satana amatulutsa Satana, ndiye kuti wagawanika. Nanga tsopano ufumu wake ungakhalepo bwanji? 27 Komanso ngati ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu za Belezebule, nanga otsatira anu amazitulutsa ndi mphamvu za ndani? Nʼchifukwa chake otsatira anuwo adzakuweruzani kuti ndinu olakwa. 28 Koma ngati ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya mzimu wa Mulungu, ndiye kuti Ufumu wa Mulungu wakufikirani modzidzimutsa.+ 29 Kapena munthu angalowe bwanji mʼnyumba ya munthu wamphamvu nʼkumulanda katundu wake, ngati choyamba atapanda kumanga munthu wamphamvuyo? Akatero mʼpamene angathe kutenga katundu mʼnyumbamo.

  • Luka 11:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Koma ena mwa iwo ananena kuti: “Ameneyu amatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebule,* wolamulira ziwanda.”+

  • Yohane 8:48
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 48 Ayudawo anamuyankha kuti: “Kodi tikunama tikamanena kuti, ‘Ndiwe Msamariya+ ndipo uli ndi chiwandaʼ?”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena