Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 33
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Mose anadalitsa mafuko (1-29)

        • Manja a Yehova “omwe adzakhalapo mpaka kalekale” (27)

Deuteronomo 33:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:28

Deuteronomo 33:2

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “anali ndi oyera ake masauzande masauzande.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:18
  • +Hab 3:3
  • +Da 7:10; Yuda 14
  • +Sl 68:17

Deuteronomo 33:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 7:8; Ho 11:1
  • +Eks 19:6
  • +Eks 19:23
  • +Eks 20:19

Deuteronomo 33:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 24:8
  • +De 4:8; Mac 7:53

Deuteronomo 33:5

Mawu a M'munsi

  • *

    Kutanthauza “Wolungama.” Limeneli ndi dzina laulemu la Isiraeli.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 44:2
  • +Eks 18:25; 19:7
  • +Nu 1:44, 46

Deuteronomo 33:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:3
  • +Nu 26:7; Yos 13:15

Deuteronomo 33:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “wamenyera nkhondo.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:8; 1Mb 5:2
  • +Sl 78:68
  • +Owe 1:2; 2Sa 7:8, 9

Deuteronomo 33:8

Mawu a M'munsi

  • *

    Mawu akuti “wanu” ndi “inu” akuimira Mulungu.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:5; Nu 3:12
  • +Eks 28:30; Le 8:6, 8
  • +Eks 32:26
  • +Eks 17:7
  • +Nu 20:13

Deuteronomo 33:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 32:27; Le 10:6, 7
  • +Mki 2:4, 5

Deuteronomo 33:10

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmphuno mwanu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 17:9
  • +2Mb 17:8, 9; Mki 2:7
  • +Eks 30:7; Nu 16:40
  • +Le 1:9

Deuteronomo 33:11

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “ziuno za.”

Deuteronomo 33:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:27

Deuteronomo 33:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:22
  • +Yos 16:1
  • +Ge 49:25

Deuteronomo 33:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 26:5; Sl 65:9

Deuteronomo 33:15

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “mʼmapiri a kumʼmawa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yos 17:17, 18

Deuteronomo 33:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 8:7, 8
  • +Eks 3:4; Mac 7:30
  • +Ge 37:7; 49:26; 1Mb 5:1, 2

Deuteronomo 33:17

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “adzagunda.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 48:19, 20

Deuteronomo 33:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:13
  • +Ge 49:14

Deuteronomo 33:19

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “adzayamwa chuma chochuluka.”

Deuteronomo 33:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:19
  • +Yos 13:24-28

Deuteronomo 33:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 32:1-5
  • +Yos 22:1, 4

Deuteronomo 33:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:16
  • +Owe 13:2, 24; 15:8, 20; 16:30
  • +Yos 19:47

Deuteronomo 33:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:21

Deuteronomo 33:24

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “asambitse.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 49:20

Deuteronomo 33:25

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “mkuwa.”

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mphamvu zako zidzafanana ndi masiku a moyo wako.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 8:7, 9

Deuteronomo 33:26

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 15:11
  • +Yes 44:2
  • +Sl 68:32-34

Deuteronomo 33:27

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 46:11; 91:2
  • +Yes 40:11
  • +De 9:3
  • +De 31:3, 4

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    11/2021, ptsa. 6-7

    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu,

    9/2021, tsa. 2

    Nsanja ya Olonda,

    10/1/1991, tsa. 13

Deuteronomo 33:28

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 8:7, 8
  • +De 11:11

Deuteronomo 33:29

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “pamalo awo okwezeka.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 33:12; 144:15; 146:5
  • +De 4:7; 2Sa 7:23; Sl 147:20
  • +Sl 27:1; Yes 12:2
  • +Sl 115:9
  • +Sl 66:3

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 33:1Ge 49:28
Deut. 33:2Eks 19:18
Deut. 33:2Hab 3:3
Deut. 33:2Da 7:10; Yuda 14
Deut. 33:2Sl 68:17
Deut. 33:3De 7:8; Ho 11:1
Deut. 33:3Eks 19:6
Deut. 33:3Eks 19:23
Deut. 33:3Eks 20:19
Deut. 33:4Eks 24:8
Deut. 33:4De 4:8; Mac 7:53
Deut. 33:5Yes 44:2
Deut. 33:5Eks 18:25; 19:7
Deut. 33:5Nu 1:44, 46
Deut. 33:6Ge 49:3
Deut. 33:6Nu 26:7; Yos 13:15
Deut. 33:7Ge 49:8; 1Mb 5:2
Deut. 33:7Sl 78:68
Deut. 33:7Owe 1:2; 2Sa 7:8, 9
Deut. 33:8Ge 49:5; Nu 3:12
Deut. 33:8Eks 28:30; Le 8:6, 8
Deut. 33:8Eks 32:26
Deut. 33:8Eks 17:7
Deut. 33:8Nu 20:13
Deut. 33:9Eks 32:27; Le 10:6, 7
Deut. 33:9Mki 2:4, 5
Deut. 33:10De 17:9
Deut. 33:102Mb 17:8, 9; Mki 2:7
Deut. 33:10Eks 30:7; Nu 16:40
Deut. 33:10Le 1:9
Deut. 33:12Ge 49:27
Deut. 33:13Ge 49:22
Deut. 33:13Yos 16:1
Deut. 33:13Ge 49:25
Deut. 33:14Le 26:5; Sl 65:9
Deut. 33:15Yos 17:17, 18
Deut. 33:16De 8:7, 8
Deut. 33:16Eks 3:4; Mac 7:30
Deut. 33:16Ge 37:7; 49:26; 1Mb 5:1, 2
Deut. 33:17Ge 48:19, 20
Deut. 33:18Ge 49:13
Deut. 33:18Ge 49:14
Deut. 33:20Ge 49:19
Deut. 33:20Yos 13:24-28
Deut. 33:21Nu 32:1-5
Deut. 33:21Yos 22:1, 4
Deut. 33:22Ge 49:16
Deut. 33:22Owe 13:2, 24; 15:8, 20; 16:30
Deut. 33:22Yos 19:47
Deut. 33:23Ge 49:21
Deut. 33:24Ge 49:20
Deut. 33:25De 8:7, 9
Deut. 33:26Eks 15:11
Deut. 33:26Yes 44:2
Deut. 33:26Sl 68:32-34
Deut. 33:27Sl 46:11; 91:2
Deut. 33:27Yes 40:11
Deut. 33:27De 9:3
Deut. 33:27De 31:3, 4
Deut. 33:28De 8:7, 8
Deut. 33:28De 11:11
Deut. 33:29Sl 33:12; 144:15; 146:5
Deut. 33:29De 4:7; 2Sa 7:23; Sl 147:20
Deut. 33:29Sl 27:1; Yes 12:2
Deut. 33:29Sl 115:9
Deut. 33:29Sl 66:3
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 33:1-29

Deuteronomo

33 Tsopano awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu woona, ananena asanafe kuti Aisiraeli adzalandira.+ 2 Iye anati:

“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai,+

Anawala pa iwo kuchokera ku Seiri.

Anawala mwa ulemerero kuchokera kudera lamapiri la Parana,+

Ndipo anali ndi angelo ake ambirimbiri,*+

Kudzanja lake lamanja kunali asilikali ake.+

 3 Iye ankakonda anthu ake,+

Anthu oyera onsewa ali mʼmanja mwanu.+

Iwowa anakhala pamapazi anu.+

Anayamba kumvetsera mawu anu.+

 4 (Mose anatipatsa chilamulo,+

Chimene ndi chuma cha mpingo wa Yakobo.)+

 5 Mulungu anakhala mfumu mu Yesuruni,*+

Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana pamodzi,+

Limodzi ndi mafuko onse a Isiraeli.+

 6 Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,+

Ndipo anthu ake asakhale ochepa.”+

 7 Iye ananena kuti Yuda adzalandira madalitso otsatirawa:+

“Inu Yehova, imvani mawu a Yuda,+

Ndipo mumubwezere kwa anthu ake.

Iye wateteza* zinthu zake ndi manja ake,

Mumuthandize kulimbana ndi adani ake.”+

 8 Ponena za Levi anati:+

“Tumimu ndi Urimu wanu*+ ndi za munthu wokhulupirika kwa inu,+

Amene munamuyesa pa Masa.+

Munayamba kulimbana naye pafupi ndi madzi a ku Meriba.+

 9 Munthu amene anauza bambo ndi mayi ake kuti, ‘Sindinasonyeze kuti ndikuwalabadira.’

Ngakhale abale ake sanawasamale,+

Ndipo ana ake anakhala ngati sakuwadziwa.

Chifukwa anatsatira mawu anu,

Ndipo anasunga pangano lanu.+

10 Amenewa azilangiza Yakobo pa zigamulo zanu+

Ndi Isiraeli mʼChilamulo chanu.+

Azipereka nsembe zofukiza kuti zikhale kafungo kosangalatsa kwa inu,*+

Ndi nsembe yathunthu paguwa lanu lansembe.+

11 Inu Yehova dalitsani mphamvu zake,

Ndipo mukondwere ndi ntchito ya manja ake.

Muphwanye miyendo ya* amene akumuukira,

Kuti amene amadana naye asathenso kuimirira.”

12 Ponena za Benjamini anati:+

“Wokondedwa wa Yehova azikhala wotetezedwa ndi iye,

Pamene akumuteteza tsiku lonse,

Iye adzakhala pakati pa mapewa ake.”

13 Ponena za Yosefe anati:+

“Dziko lake lidalitsidwe ndi Yehova.+

Lidalitsidwe ndi zinthu zabwino kwambiri zakumwamba,

Ndi mame komanso madzi ochokera mu akasupe a pansi pa nthaka.+

14 Lidalitsidwenso ndi zinthu zabwino kwambiri, zochokera ku dzuwa,

Ndi zokolola zabwino kwambiri mwezi uliwonse,+

15 Lidalitsidwe ndi zinthu zabwino koposa zamʼmapiri akale,*+

Ndi zinthu zabwino kwambiri zamʼmapiri amene adzakhalapo mpaka kalekale.

16 Lidalitsidwe ndi zinthu zabwino kwambiri za padziko lapansi, ndi chuma chake chonse,+

Komanso movomerezedwa ndi Iye amene anaonekera mʼchitsamba chaminga.+

Madalitso amenewa akhale pamutu pa Yosefe,

Paliwombo pa munthu amene anasankhidwa pakati pa abale ake.+

17 Ulemerero wake ndi wofanana ndi wa mwana wa ngʼombe wamphongo woyamba kubadwa,

Ndipo nyanga zake ndi nyanga za ngʼombe yamphongo yamʼtchire.

Nyanga zimenezo adzakankha* nazo anthu.

Adzakankha nazo anthu onse pamodzi mpaka kukafika kumalekezero a dziko lapansi.

Nyanga zimenezo ndi anthu masauzande makumimakumi a fuko la Efuraimu,+

Ndiponso anthu masauzande a fuko la Manase.”

18 Ponena za Zebuloni anati:+

“Kondwera Zebuloni iwe, pa maulendo ako,

Ndiponso iwe Isakara, mʼmatenti ako.+

19 Adzaitanira mitundu ya anthu kuphiri.

Kumeneko adzapereka nsembe zachilungamo.

Chifukwa adzatenga chuma* kuchokera pa chuma chochuluka cha mʼnyanja,

Ndi chuma chobisika chamumchenga.”

20 Ponena za Gadi anati:+

“Wofutukula malire a dera la Gadi ndi wodala.+

Iye adzagona kumeneko ngati mkango,

Wokonzeka kukhadzula dzanja, komanso kungʼamba mutu paliwombo.

21 Iye adzasankha gawo labwino kwambiri kuti likhale lake,+

Chifukwa gawo loperekedwa ndi wopereka malamulo linasungidwa kumeneko.+

Atsogoleri a anthu adzasonkhana pamodzi.

Iye adzachita chilungamo cha Yehova,

Ndi zigamulo zake zokhudza Isiraeli.”

22 Ponena za Dani anati:+

“Dani ndi mwana wa mkango.+

Adzadumpha kuchokera ku Basana.”+

23 Ponena za Nafitali anati:+

“Nafitali wakhutira chifukwa chovomerezedwa,

Ndipo madalitso a Yehova amuchulukira.

Tenga chigawo chakumadzulo ndi kumʼmwera.”

24 Ponena za Aseri anati:+

“Aseri anamudalitsa ndi ana aamuna.

Abale ake amukomere mtima,

Ndipo apondetse* mapazi ake mʼmafuta.

25 Chitsulo komanso kopa* ndi zokhomera geti lako,+

Ndipo udzakhala wotetezeka masiku onse a moyo wako.*

26 Palibe amene angafanane ndi Mulungu woona+ wa Yesuruni,+

Amene amayenda mumlengalenga kuti akuthandize,

Amene amayenda pamitambo mu ulemerero wake.+

27 Mulungu ndi malo ako othawirapo kuyambira kalekale,+

Iye wakunyamula mʼmanja ake omwe adzakhalapo mpaka kalekale.+

Adzathamangitsa mdani pamaso pako,+

Ndipo adzanena kuti, ‘Awonongeni!’+

28 Isiraeli adzakhala motetezeka,

Kasupe wa Yakobo adzakhala motetezeka,

Mʼdziko lokhala ndi chakudya komanso vinyo watsopano,+

Limene kumwamba kwake kudzagwetsa mame.+

29 Ndiwe wosangalala iwe Isiraeli!+

Ndani angafanane ndi iwe,+

Anthu amene akupulumutsidwa ndi Yehova,+

Chishango chako chokuteteza,+

Komanso lupanga lako lamphamvu?

Adani ako adzakhala mwamantha chifukwa cha iwe,+

Ndipo iwe udzaponda pamisana yawo.”*

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena