Yesaya
4 Tsiku limenelo, akazi 7 adzagwira mwamuna mmodzi+ nʼkumuuza kuti:
“Ife tizidya chakudya chathu
Ndipo tizidzipezera tokha zovala.
Inuyo mungotilola kuti tizitchedwa ndi dzina lanu
2 Tsiku limenelo, chinthu chimene Yehova adzachiphukitse chidzakhala chokongola komanso chaulemerero. Zipatso za mʼdzikolo zidzakhala zonyaditsa ndi zokongola kwa Aisiraeli amene adzapulumuke.+ 3 Aliyense amene adzatsale mu Ziyoni ndiponso amene adzasiyidwe mu Yerusalemu adzatchedwa woyera, anthu onse a mu Yerusalemu amene analembedwa mayina kuti akhale ndi moyo.+
4 Yehova akadzatsuka nyansi* za ana aakazi a Ziyoni+ ndiponso akadzatsuka magazi amene Yerusalemu anakhetsa, pogwiritsa ntchito mzimu wa chiweruzo komanso mzimu woyaka moto,+ 5 malo onse a paphiri la Ziyoni ndi malo onse a mu Yerusalemu ochitirapo misonkhano, Yehova adzawapangira mtambo ndi utsi kuti ziziwathandiza masana. Adzawapangiranso moto wowala walawilawi kuti uziwathandiza usiku,+ ndipo pamwamba pa malo onse aulemererowo padzakhala chotchinga. 6 Padzakhalanso msasa kuti uzipereka mthunzi woteteza ku dzuwa masana,+ ndiponso kuti ukhale malo othawirapo komanso achitetezo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mvula.+