Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w90 2/1 tsamba 31
  • Kuchitira Umboni M’malo Abizinezi—Njira Yachijapan

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuchitira Umboni M’malo Abizinezi—Njira Yachijapan
  • Nsanja ya Olonda​—1990
  • Nkhani Yofanana
  • Lalikirani Uthenga Wabwino Paliponse
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
  • Mmene Tingalalikirire M’gawo la Malonda
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Gwiritsirani Ntchito Magazini Athu m’Njira Yabwino Koposa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Anthu a ku Japan Analandira Mphatso
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda​—1990
w90 2/1 tsamba 31

Kuchitira Umboni M’malo Abizinezi​—Njira Yachijapan

LAMULO la Yesu Kristu la kupereka ntchito yolalikira ku “malekezero ake a dziko” liyenera kuphatikiza malo abizinezi. (Machitidwe 1:8) Mu Japan, kupereka umboni Waufumu kwa anthu omagwira ntchito m’malo apoyera ndi m’maofesi a makampani aakulu kumapereka chitokoso. Ofalitsa Aufumu mu mpingo wina anatenga chilolezo kuchita umboni wamagazine m’nyumba ya maofesi a mzinda mkati mwa kupuma kwa chakudya chamasana. Ofalitsawo sanangopemphera kwa Yehova kuwapatsa kulimba mtima komanso anapereka chisamaliro chachikulu ku kavalidwe ndi makhalidwe awo ndipo anapanga makadi ovala osonyeza maina awo ndi kuwadziŵikitsa monga Mboni za Yehova.

Mboni inkafikira wantchito, mwakunena kuti: “Zikomo, ndinapatsidwa chilolezo kulankhula kwa anthu pano. Kodi mungalole kumvetsera kwa ine pamene mukudya?” Mboniyo inafunikira kusonyeza chiweruzo chabwino ndi kugwiritsira ntchito mawu “okometsedwa ndi mchere.” (Akolose 4:6, NW) Pa ulendo wawo woyamba, iwo anagaŵira magazine 39, koma kunawatengera maulendo anayi kuti akwaniritse nyumba yonseyo ya nyumba zosanjikana zisanu ndi zitatu mmene anthu 1,500 amagwiramo ntchito. Iwo anagaŵira chiwonkhetso cha magazine oposa pa zana limodzi ndipo anali okhoza kuyamba njira za magazine ndi kupanga maulendo obwereza.

Mmodzi wa ofalitsawo anapanga ulendo wobwereza kwa manijala. Pamene iye anamva lemba la mu New World Translation likuŵerengedwa, ananena kuti: “Baibulo ili nlosavuta kumvetsetsa. Lomwe ndinaŵerengapo linali m’Chijapanese chakale ndipo linali lovuta kwenikweni kuŵerenga.” Kope la New World Translation linaperekedwa kwa iye mlungu wotsatira.

Kodi mungachite zowonjezereka m’gawo la mpingo wanu kulalikira mbiri yabwino kwa “anthu onse,” kuphatikizapo aja a m’madera abizinezi?​—Yerekezerani ndi 1 Timoteo 2:4.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena