Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/05 tsamba 6
  • Yesani Ulaliki Wosavuta Kuusintha

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesani Ulaliki Wosavuta Kuusintha
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Zitsanzo za Maulaliki a Utumiki wa Kumunda
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Tiyeni ‘Tinene Mfundo Yathu Mwachidule!’
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Mawu Oyambirira Ogwiritsira Ntchito mu Uminisitala Wakumunda
    Kukambitsirana za m’Malemba
  • Kulalikira Uthenga Wabwino ndi Maganizo Otsimikiza
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
km 1/05 tsamba 6

Yesani Ulaliki Wosavuta Kuusintha

Kuchita chidwi ndi anthu kudzatithandiza kuti tiyesetse kuzindikira mavuto awo ndi kuwasonyeza mmene Ufumu udzathetsere mavuto onse amene akukumana nawo. (Afil. 2:4) Ulaliki wosavuta umene ofalitsa ena auona kukhala wogwira mtima ndi wom’pempha mwininyumba kufotokoza maganizo ake pa zithunzi za Paradaiso za m’mabuku athu, pamasamba osonyezedwa pamwambapa kulamanja kwa tsamba lino. Mukhoza kuchita zimenezi pogwiritsa ntchito ena mwa mawu oyamba otsatirawa:

◼ “Kodi mukuganiza kuti tidzaonadi anthu akusangalala ndi moyo ngati uyu umene ausonyeza apawu?”

◼ “Tonsefe tingakonde kuti ana anthu asangalale ndi dziko ngati ili alisonyeza apali. Kodi mukuganiza kuti n’chiyani chikufunika kuti dziko ngati limeneli likhalepo?”

◼ “Ichi ndi chitsanzo chosonyeza mmene dziko lizidzaonekera chifuno cha Mulungu chikadzachitika pano padziko lapansi monga kumwamba. Kodi mukuonapo chilichonse chimene chikusiyana ndi moyo wamasiku anowu?”

◼ “Kodi mukufuna kudzakhala ndi moyo m’dziko ili alisonyeza apali. [Yembekezani ayankhe.] Kodi mukuganiza kuti zimenezi zidzachitika m’nthawi yathu ino?”

Mvetserani mwatcheru mayankho a munthuyo, ndipo mwaulemu m’funseni funso lina lowonjezera kapena awiri kuti mudziwe maganizo ake. Ngati ena angayankhe kuti sakufuna kudzakhala ndi moyo m’dziko limene alisonyezalo kapena kuti sakhulupirira kuti zimenezo zingatheke, musafulumire kugamula kuti alibe chidwi. Yesani kuwafunsa mwanzeru chifukwa chimene amaganizira mmene akuneneramo. Zimene angayankhe pamenepo zikhoza kuvumbula nkhawa yaikulu imene ali nayo chifukwa cha mavuto ochuluka omwe anthu akulephera kuwathetsa amene anthu onse akukumana nawo.—Ezek. 9:4.

Mukadziwa mavuto amene mwininyumba ali nawo, sinthani ulaliki wanu mogwirizana ndi mavuto akewo. M’sonyezeni mfundo yaikulu ya uthenga wa Ufumu imene ikukhudza mavuto akewo mwachindunji. Werengani lemba limodzi kapena awiri amene akukhudza vuto limene akuda nalo nkhawalo. (Onani mfundo zimene zili kudzanja lamanjazo.) Muloleni adzionere yekha zimene Mawu a Mulungu amanena. Ngati waonetsa chidwi, gawirani buku ndi kukonza zoti mudzabwerenso. Pitirizani kukulitsa chidwi chimene anachionetsa pa kukambirana kwanu koyamba.

[Bokosi patsamba 6]

Zitsanzo za Zithunzi za Paradaiso

Buku la Mphunzitsi Waluso: masamba 251 mpaka 254

Buku la Chidziŵitso: masamba 4 ndi 5, 188 ndi 189

Bulosha la Mulungu Amafunanji: masamba 11 ndi 13

Buku la Mtendere Weniweni: tsamba 98

Buku la Lambirani Mulungu: masamba 92 ndi 93

[Bokosi patsamba 6]

Zimene Anthu Amada Nazo Nkhawa

Boma losathandiza

Salmo 146:3, 4;

Danieli 2:44

Chinyengo, kusowa chilungamo

Yesaya 9:6, 7;

2 Petro 3:13

Imfa, kulira

Yesaya 25:8;

Chivumbulutso 21:3, 4

Kuchitira nkhanza nyama

Miyambo 12:10

Kutha kwa makhalidwe abwino

2 Timoteo 3:1-5

Kuvutika maganizo

Salmo 34:8;

Yesaya 65:17-19

Kuwononga dziko

Chivumbulutso 11:18

Matenda, kulumala

Yesaya 33:24; 35:5, 6

Njala, kusowa kwa zakudya m’thupi

Salmo 72:16;

Yesaya 25:6

Nkhondo, uchigawenga

Salmo 46:8, 9;

Mika 4:3, 4

Nyumba, mavuto a zachuma

Yesaya 65:21, 22

Tsankho

Yesaya 11:3-5;

Machitidwe 10:34, 35

Umphawi, kuponderezana

Salmo 72:12-14;

Mlaliki 8:9

Upandu, chiwawa

Salmo 37:10, 11;

Miyambo 2:21, 22

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena