Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/14 tsamba 4
  • Ndandanda ya Mlungu wa April 7

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ndandanda ya Mlungu wa April 7
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Timitu
  • MLUNGU WOYAMBIRA APRIL 7
Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
km 3/14 tsamba 4

Ndandanda ya Mlungu wa April 7

MLUNGU WOYAMBIRA APRIL 7

Nyimbo Na. 6 ndi Pemphero

Phunziro la Baibulo la Mpingo:

jr mutu 10 ndime 1-7 (Mph. 30)

Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:

Kuwerenga Baibulo: Ekisodo 7–10 (Mph. 10)

Na. 1: Ekisodo 9:20-35 (Osapitirira mph. 4)

Na. 2: Mmene Kubweranso kwa Yesu Kudzakhalire Ndiponso Mmene Diso Lililonse Lidzamuonere—rs tsa. 163 ndime 3–tsa. 164 ndime 4 (Mph. 5)

Na. 3: Muzikhala Wokhulupirika Ndiponso Wokonzeka Kuthandiza Abale Anu—lv tsa. 33-34 ndime 16-18 (Mph. 5)

Msonkhano wa Utumiki:

Nyimbo Na. 124

Mph. 10: Zimene Munganene Pogawira Magazini a April. Nkhani yokambirana. Yambani ndi kuchita chitsanzo cha mmene tingagawirire magaziniwo pogwiritsa ntchito zitsanzo za ulaliki zimene zili patsamba lino. Kenako kambiranani chitsanzo cha ulaliki chilichonse kuyambira poyambirira mpaka pamapeto. Pomaliza, limbikitsani ofalitsa kuti awerenge ndi kudziwa bwino nkhani za m’magaziniwa komanso kuti adzagawire nawo.

Mph. 10: Musaiwale Kuchereza Alendo. (Aheb. 13:1, 2) Nkhani yokambidwa ndi mkulu. Kumbutsani mpingo zomwe zakonzedwa kudzachitika pa nyengo ya Chikumbutso. Fotokozani njira zimene tingadzasonyezere kuchereza alendo komanso ofalitsa ofooka amene adzafike pa mwambowu. Chitani chitsanzo cha mbali ziwiri. Chitsanzo choyamba chisonyeze wofalitsa akulandira munthu amene analandira kapepala komuitanira ku Chikumbutso. Chitsanzo chachiwiri chisonyeze wofalitsayo, pambuyo pa mwambowu akukonza zoti adzakumanenso ndi munthu uja.

Mph. 10: Kodi Tinachita Zotani? Nkhani yokambirana. Pemphani omvera kuti afotokoze mmene anapindulira pogwiritsa ntchito malangizo a m’nkhani yakuti, “Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Zimene Tinganene kwa Anthu Amene Sakufuna Kuti Tiwalalikire.” Kenako apempheni kuti anene zinthu zosangalatsa zimene anakumana nazo.

Nyimbo Na. 20 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena