Pitanibe Patsogolo
KODI mwayesa kugwiritsa ntchito maluso onse a kulankhula amene mwaphunzira mu sukuluyi? Kodi mwatsiriza zochita zoperekedwazo? Kodi mumagwiritsa ntchito luso lililonse pokamba nkhani zanu, kaya m’sukuluyi kapena pamisonkhano ina, komanso mu utumiki wa kumunda?
Pitirizani kupindula ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu. Kaya mwakhala mukukamba nkhani kwa utali wotani, zilipo mbali zimene mungapitebe nazo patsogolo.