Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w10 1/1 tsamba 30-31
  • Munthu Wodzichepetsa Ndiponso Wolimba Mtima

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Munthu Wodzichepetsa Ndiponso Wolimba Mtima
  • Nsanja ya Olonda—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Tikuphunzira pa Chifundo cha Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Sanagonje Poyesedwa
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2010
w10 1/1 tsamba 30-31

Zoti Achinyamata Achite

Munthu Wodzichepetsa Ndiponso Wolimba Mtima

YONA​—GAWO 1

Malangizo: Chitani zotsatirazi muli pamalo opanda phokoso. Pamene mukuwerenga mavesiwo, yerekezerani kuti nkhaniyo ikuchitika inuyo muli pomwepo. Yesani kuona m’maganizo mwanu zimene zikuchitika. Mukhale ngati mukumva zimene anthuwo akulankhula. Yesani kumva mmene anthu a m’nkhaniyi akumvera.

1 ONANI NKHANIYI BWINOBWINO.​—WERENGANI YONA 1:1-17; 2:10–3:5.

Kodi mukuganiza kuti panyanjapo pankaoneka bwanji ndiponso pankamveka phokoso lotani chifukwa cha mphepo yamkutho?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti zimene Yona ndiponso anthu oyendetsa chombocho ananena zikusonyeza kuti ankamva bwanji mumtima mwawo?

․․․․․

Fotokozani zimene Yona ayenera kuti ankaganiza panthawi imene ankamira m’nyanja ndiponso ali m’mimba mwa chinsomba. (Werengani Yona 2:1-9.)

․․․․․

2 FUFUZANI MOZAMA.

Kodi ku Nineve kunkakhala anthu otani, nanga n’chifukwa chiyani poyamba Yona sanafune kuwalalikira anthu amenewa? (Nahumu 3:1)

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Mulungu ankaona kuti Nineve unali “mudzi waukulu pamaso” pake? (Yona 3:3; 2 Petulo 3:9)

․․․․․

Popeza kuti Yona ananena zoona zokhazokha za tchimo lake ndiponso za Mulungu, kodi zimenezi zikusonyeza kuti iye anali munthu wotani? (Werenganinso Yona 1:9, 10.)

․․․․․

Kodi Yona ayenera kuti anadziwa bwanji zimene zinachitika m’chombocho iye ataponyedwa m’nyanja? (Werenganinso Yona 1:15, 16.)

․․․․․

3 GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA PONENA ZA . . 

Mantha.

․․․․․

Kudzichepetsa.

․․․․․

Kulimba mtima.

․․․․․

Mmene Yehova amaonera anthu ngakhale amene timawaona kuti ndi oipa kwambiri.

․․․․․

4 M’NKHANIYI, KODI NDI MFUNDO ITI IMENE YAKUKHUDZANI KWAMBIRI NDIPO N’CHIFUKWA CHIYANI?

․․․․․

Kuti mudziwe zambiri, werengani Nsanja ya Olonda ya January 1, 2009, tsamba 25-28.

NGATI MULIBE BAIBULO, MUNGAWERENGE LA PA INTANETI PA WEBUSAITI YATHU YA www.jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena