Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w10 3/1 tsamba 24-25
  • Zimene Tikuphunzira pa Chifundo cha Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimene Tikuphunzira pa Chifundo cha Mulungu
  • Nsanja ya Olonda—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Munthu Wodzichepetsa Ndiponso Wolimba Mtima
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2010
w10 3/1 tsamba 24-25

Zoti Achinyamata Achite

Zimene Tikuphunzira pa Chifundo cha Mulungu

YONA​—GAWO 2

Malangizo: Chitani zotsatirazi muli pamalo opanda phokoso. Pamene mukuwerenga mavesiwo, yerekezerani kuti nkhaniyo ikuchitika inuyo muli pomwepo. Yesani kuona m’maganizo mwanu zimene zikuchitika. Mukhale ngati mukumva zimene anthuwo akulankhula. Yesani kumva mmene anthu a m’nkhaniyi akumvera.

1 ONANI NKHANIYI BWINOBWINO​—WERENGANI YONA 3:1–4:11.

Kodi mukuganiza kuti Yona ankamva bwanji mumtima mwake pamene amalowa mumzinda wa Nineve?

․․․․․

Malinga ndi zimene Yona ananena polengeza chiweruzo cha Yehova, kodi mukuganiza kuti ankamva bwanji mumtima mwake?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Yona anavutika bwanji panthawi imene anakhala pansi kunja kwa mzinda? (Onani Yona 4:5-8.)

․․․․․

2 FUFUZANI MOZAMA.

Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Yona anafuna kuti Yehova awononge mzinda wa Nineve, pokwaniritsa chenjezo limene anapereka?

․․․․․

Pogwiritsa ntchito mabuku omwe mungafufuzemo zinthu, fufuzani za (1) maonekedwe a mtengo wa msatsi ndi (2) tanthauzo la zimene mfumu ya ku Nineve inachita pofunda chiguduli ndiponso kukhala paphulusa.

․․․․․

Ngakhale kuti poyamba sanafune kukachita zimene Mulungu anam’tuma ku Nineve, n’chifukwa chiyani tinganenebe kuti Yona anali mneneri wokhulupirika komanso wolimba mtima? (Mateyo 21:28-31)

․․․․․

3 GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA ZOKHUDZA  . . .

Mfundo yakuti anthu angathe kusintha n’kusiya kuchita zoipa.

․․․․․

Chifundo cha Yehova.

․․․․․

Kufunika kokhala achifundo.

․․․․․

4 M’NKHANIYI, KODI NDI MFUNDO ITI IMENE YAKUKHUDZANI KWAMBIRI, NDIPO N’CHIFUKWA CHIYANI?

․․․․․

Kuti mudziwe zambiri, werengani Nsanja ya Olonda ya April 1, 2009, tsamba 14 mpaka 18.

NGATI MULIBE BAIBULO, MUNGAWERENGE LA PA INTANETI PA WEBUSAITI YATHU YA www.jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena