Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w10 9/1 tsamba 30-31
  • Mulungu Alibe Tsankho

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mulungu Alibe Tsankho
  • Nsanja ya Olonda—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Achiritsa Anthu Mozizwitsa
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Anagometsa Anthu ndi Mawu Ake
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Yesu Sanagonje Poyesedwa
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2010
w10 9/1 tsamba 30-31

Zoti Achinyamata Achite

Mulungu Alibe Tsankho

Malangizo: Chitani zotsatirazi muli pamalo opanda phokoso. Pamene mukuwerenga mavesiwo, yerekezerani kuti nkhaniyo ikuchitika inuyo muli pomwepo. Yesani kuona m’maganizo mwanu zimene zikuchitika. Mukhale ngati mukumva zimene anthuwo akulankhula. Yesani kumva mmene anthu a m’nkhaniyi akumvera mumtima mwawo.

Amene akutchulidwa kwambiri m’nkhaniyi: Koneliyo ndi Petulo.

Chidule cha nkhaniyi: Petulo anatsatira chitsanzo cha Mulungu polalikira mopanda tsankho kwa Koneliyo amene sanali Myuda.

1 ONANI NKHANIYI BWINOBWINO.​—WERENGANI MACHITIDWE 10:1-35, 44-48.

Kodi mukuganiza kuti Koneliyo ankaoneka bwanji? Fotokozani.

․․․․․

Mogwirizana ndi zimene zinalembedwa pamavesi 3 mpaka 6, kodi mukuganiza kuti Koneliyo ankamva bwanji pamene ankalankhulana ndi mngelo?

․․․․․

Kodi mukuganiza kuti Koneliyo anakambirana zotani ndi antchito ake, mogwirizana ndi zimene mavesi 7 ndi 8 akunena?

․․․․․

2 FUFUZANI MOZAMA.

N’chifukwa chiyani masomphenya amene Mulungu anapatsa Petulo m’mavesi 10 mpaka 16 anamuthandiza kusintha maganizo ake? (Zokuthandizani: Ganizirani zimene Petulo ankaganiza poyamba chifukwa chakuti anali Myuda, malinga ndi zimene vesi 14 likunena.)

․․․․․

Kodi mukuona khalidwe liti la Koneliyo mu vesi 25? N’chifukwa chiyani anthu ambiri amene ali ndi udindo sakhala ndi khalidwe limeneli? (Zokuthandizani: Onani vesi 1.)

․․․․․

Pogwiritsa ntchito mabuku ofufuzira amene muli nawo, fufuzani kuti mudziwe kuchuluka kwa gulu la asilikali a Italiya limene Koneliyo ankaliyang’anira.

․․․․․

N’chifukwa chiyani mfundo yoti Koneliyo anakhala Mkhristu ndi yochititsa chidwi?

․․․․․

3 GWIRITSANI NTCHITO ZIMENE MWAPHUNZIRA. LEMBANI ZIMENE MWAPHUNZIRA ZOKHUDZA . . .

Kugwiritsa ntchito mafanizo mogwira mtima.

․․․․․

Kupanda tsankho kwa Mulungu.

․․․․․

Zimene inuyo mungachite kuti mupewe kuchita zinthu mwatsankho.

․․․․․

4 M’NKHANIYI, KODI NDI MFUNDO ITI IMENE YAKUKHUDZANI MTIMA KWAMBIRI, NDIPO N’CHIFUKWA CHIYANI?

․․․․․

NGATI MULIBE BAIBULO, MUNGAWERENGE LA PA INTANETI PA WEBUSAITI YATHU YA www.jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena