Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/99 tsamba 7
  • Kodi Muli ndi Oda Yokhazikika ya Magazini?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Muli ndi Oda Yokhazikika ya Magazini?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Gawirani Magazini mu Utumiki Wanu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Gwiritsirani Ntchito Magazini Athu m’Njira Yabwino Koposa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Magazini Amalengeza Ufumu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • ‘Kumayenda Mnjira ya Chowonadi’
    Nsanja ya Olonda—1987
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 4/99 tsamba 7

Kodi Muli ndi Oda Yokhazikika ya Magazini?

1 Kodi munayamba mwapita kumsonkhano wa utumiki wakumunda ndi kupeza kuti m’chikwama chanu mulibiretu magazini? Chabwino, kumbukirani mphatika ya mutu wakuti “Gwiritsirani Ntchito Magazini Athu m’Njira Yabwino Koposa,” yopezeka mu Utumiki Wathu Waufumu wa September 1995. Inatiuza ‘kukhala ndi oda yoikika ya magazini,’ ikumati: “Lembetsani oda yokuyenerani kwa mbale wosamalira magazini ya unyinji wodziŵika wa makope a magazini alionse. M’njira imeneyi, inu ndi banja lanu mudzakhala mukulandira magazini okwanira mokhazikika.” Kodi mwachita zimenezi?

2 Bwanji osalembetsa oda yokhazikika ya magazini? Mudzakakamizika kugaŵira magaziniwo mlungu uliwonse, ndipo mwa kuchita zimenezi mudzapeza chimwemwe chochuluka. Ngati muli nayo kale oda yokhazikika, onani ngati chiŵerengero cha magazini amene mumalandira chikugwirizana ndi magazini amene mumafunikira mwezi uliwonse mu utumiki. N’zoona, tifunika kukhala odalirika potenga oda yathu mlungu uliwonse ndipo tiyenera kuchita zimenezo. Ngati mungachoke pampingopo kwa nthaŵi yaitali, muuzeni wosamalira magazini ngati mukufuna kuti magaziniwo aziwapereka kwa munthu wina mpaka inu mutadzabwera.

3 Mphatika imene yatchulidwa pamwambayi inanenanso kuti tiyenera “kulinganiza tsiku la magazini lokhazikika.” Kodi mudzachirikiza Tsiku la Magazini mlungu uliwonse? Monga mmene zasonyezedwera pa Kalenda ya 1999 ya Mboni za Yehova, limeneli ndi Loweruka lililonse pachaka! Musachepetse kufunika kogaŵira Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Pamene tiyesetsa kutengamo mbali mokwanira m’ntchito ya magazini, ndiye kuti ‘tikudza ndi uthenga wabwino wa zinthu zabwino’ kwa anansi athu.—Yes. 52:7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena