Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/02 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 1/02 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Jan. 15

“Anthu ambiri amagwiritsa ntchito mafano polambira. Kodi muganiza kuti zinthu ngati zimenezi zili ndi mphamvu yopulumutsa munthu? [M’yembekezeni ayankhe.] Taonani zimene Mulungu woona adzatichitira. [Ŵerengani Chivumbulutso 21:3, 4.] Amene angachite zimenezi ndi Mulungu weniweni yekha basi. Magazini iyi ikufotokoza kuti ameneyo ndi ndani komanso mapindu amene tingapeze mwa kum’khulupirira.”

Galamukani! Jan. 8

“Kodi simukuvomereza kuti tifunika chakudya chabwino ndi chodalirika kuti titeteze moyo wathu? [M’yembekezeni ayankhe.] Onani zimene Mulungu analonjeza anthu ake kalelo m’nthaŵi za m’Baibulo. [Ŵerengani Levitiko 26:4, 5.] Galamukani! ikufotokoza zinthu zimene zikudetsa nkhaŵa masiku ano pankhani ya zimene timadya. Ikunenanso za nthaŵi imene Mulungu adzatipatsa chitetezo padziko lonse.”

Nsanja ya Olonda Feb. 1

“Anthu ambiri akuda nkhaŵa chifukwa cha kuipa kwa malo. Koma kodi munaganizapo zakuti maganizo angaipenso? [M’yembekezeni ayankhe.] Baibulo limagogomeza kuti ukhondo wa thupi ndi wauzimu n’ngofunika kwambiri. [Ŵerengani 2 Akorinto 7:1.] Ndikhulupirira kuti nkhani imeneyi ikuthandizani kwambiri.”

Galamukani! Jan. 8

“Tonse tikudziŵa za tsokali limene lagwedeza dziko lonse. Kuyambira pamene zimenezi zinachitika, anthu ambiri afuna chilimbikitso ndi chithandizo chachikulu. Nkhani ino mwa zina, ikufotokoza zimene Mboni za Yehova zakhala zikuchita pothandiza anthu opulumuka pa tsoka limeneli ndi anthu othandiza ovulala ndiponso anthu amene abale awo anamwalira pa tsokali.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena