Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/03 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 1/03 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Dec. 15

“Chaka chilichonse nyengo ngati ino, anthu ambiri amakumbukira kubadwa kwa Yesu. Kodi mumadziŵa kuti pali zinthu zofunika kwambiri zimene tingaphunzire pankhani ya m’Baibulo ya kubadwa kwa Yesu? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno pitani pa tsamba 5, ndipo ŵerengani 2 Timoteo 3:16.] Nsanja ya Olonda iyi ikutchula zina mwa zinthu zimene tingaphunzirepo.”

Galamukani! Jan. 8

“Ndikukambirana ndi anthu lemba ili la Marko 10:21-23. [Ŵerengani.] Anthu ambiri akaŵerenga lemba ili amaganiza kuti Akristu sayenera kukhala anthu achuma koma amphaŵi. Nanga inu mukuganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe.] Galamukani! iyi, pankhani yakuti “Lingaliro la Baibulo,” ikufotokoza zimene Yesu anatanthauza ndi mawu ameneŵa.”

Nsanja ya Olonda Jan. 1

“Nthaŵi zambiri munthu akakhala kuti wokondedwa wake wamwalira kapena wadwala, amafunsa kuti, ‘N’chifukwa chiyani Mulungu amalola zimenezi?’ Mwina munafunsapo funso ngati limeneli. Baibulo limasonyeza kuti Mulungu amawamvera chisoni anthu ovutika. [Ŵerengani Yesaya 63:9a.] Magazini iyi ikufotokoza chifukwa chake tingakhulupirire kuti Mulungu adzathetsa mavuto.”

Galamukani! Jan. 8

“Kodi mukuganiza kuti boma liyenera kupondereza ufulu wa anthu wa kulankhula? [Yembekezani ayankhe.] Bwanji nanga ngati akulankhula ndi anzawo za chipembedzo, monga mmene pakunenera apa? [Ŵerengani Machitidwe 28:30, 31.] Posachedwapa, funso limeneli linakafika ku Khoti Lalikulu ku United States. Tikukupemphani kuŵerenga za nkhaniyi mu Galamukani! iyi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena