Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/04 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 1/04 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Jan. 15

“Chifukwa chakuti masiku ano anthu ambiri sasunga malonjezo, ambiri zimawavuta kudalira munthu aliyense. Kodi mukuganiza kuti pali amene tingadalire malonjezo ake? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Yoswa 23:14.] Magazini iyi ikusonyeza zimene tingachite kuti tizidalira malonjezo a Mulungu amene analembedwa m’Baibulo.”

Galamukani! Jan. 8

“Tonsefe timalakalaka kuona ana athu akukhala mosangalala komanso zinthu zikuwayendera bwino. Kodi mumaganiza kuti n’chiyani chomwe ana amafunikira kwambiri kuti akhale bwinobwino m’dziko la masiku ano lodzala mavutoli? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Miyambo 22:6.] Magazini ya Galamukani! iyi ikufotokoza zomwe ana amafunikira ndiponso momwe makolo angakwaniritsire zofunikazo.”

Nsanja ya Olonda Feb. 1

“Ambirife timayesetsa kusamalira thanzi lathu. Komabe, zimene anthu ena ofufuza apeza posachedwapa zikusonyeza kuti moyo wathu umadaliranso zinthu zauzimu. Kodi mukuganiza kuti zimenezi n’zoona? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Mateyu 5:3.] Magazini iyi ya Nsanja ya Olonda ikufotokoza zimene tingachite kuti tikwaniritse zosoŵa zathu zauzimu.”

Galamukani! Jan. 8

“Padziko lonse, anthu miyandamiyanda akuvutika ndi matenda osiyanasiyana a m’maganizo. Mlengi wathu amawakonda kwambiri anthu ameneŵa. [Ŵerengani Salmo 34:18.] Magazini iyi ikufotokoza mmene odwala angathandizidwire. Komanso ikutchula lonjezo la m’Baibulo loti posachedwapa matenda onse adzathetsedwa.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena