Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 5/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda May 15

“Tsiku lililonse timamva malipoti a zachiwawa. Kodi mukuganiza kuti moyo unali wotero kale? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo likunena. [Ŵerengani Mateyu 24:37.] Masiku a Nowa anali oipa kwambiri moti Mulungu anawononga anthu onse koma anasiya Nowa ndi banja lake. Magazini iyi ikufotokoza tanthauzo la zimene zinachitikazo kwa ife masiku ano.”

Galamukani! May 8

“M’dziko losintha mofulumira lino, anthu ambiri amada nkhaŵa kuti mwina ana akukula mofulumira kwambiri. Kodi inunso zimakudetsani nkhaŵa? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Mlaliki 3:1, 4.] Paubwana sinthaŵi yosamalira maudindo amene amasamalira akuluakulu. Galamukani! iyi ikufotokoza mmene makolo angatetezere ubwana wa ana awo.”

Nsanja ya Olonda June 1

“Malipoti onena za kusakaza ndalama zosonkhedwa kuti zithandize ovutika akuchititsa anthu ena kukayikira ngati chili chinthu chanzeru kupereka ndalama ku mabungwe othandiza anthu ovutika. Komabe, pali anthu ambiri ofunika thandizo. Kodi mukuganiza kuti m’pofunika kutani? [Yembekezani ayankhe. Akayankha ŵerengani Ahebri 13:16.] Magazini iyi ikufotokoza za kuthandiza kumene kumakondweretsa Mulungu.”

Galamukani! May 8

Ambirife tikudziŵa wina amene amadwala nthenda ya shuga. Kodi mumadziŵa zambiri za nthenda imeneyi? [Muonetseni chikuto cha magaziniyi, ndipo yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza zimene zimayambitsa nthendayi ndiponso mankhwala ake. Ikufotokozanso zimene Baibulo limalonjeza zothetseratu matenda onse.” Malizani ndi kuŵerenga Yesaya 33:24.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena