Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 6/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda June 15

“Anthu ena amaona kuti Yesu anali munthu wamkulu m’mbiri ya anthu. Ena amakayikira zoti anakhalako. Kodi mukuganiza kuti zimene timakhulupirira pankhani ya Yesu zili ndi ntchito? [Akayankha, ŵerengani Machitidwe 4:12.] Kodi pali umboni wanji wosonyeza kuti Yesu anakhalakodi padziko lapansi? Magazini iyi ikuyankha funso limeneli.”

Galamukani! June 8

“Masiku ano, matenda oyamba chifukwa cholumidwa ndi tizilombo ndi amodzi a zinthu zambiri zimene zikuika thanzi lathu pangozi. Kodi mukudziŵa kuti pali zimene tingachite kuti tidziteteze? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza zimene tingachite, komanso lonjezo lopezeka m’Baibulo la nthaŵi imene sipadzakhalanso matenda.” Pomaliza ŵerengani lemba la Yesaya 33:24.

Nsanja ya Olonda July 1

“Chimodzi mwa zinthu zofunika kwambiri pamoyo wa munthu ndi kusonyeza chikondi ndiponso kukondedwa. [Ŵerengani mawu a pachithunzi cha patsamba 4.] Komabe, kodi mwaona kuti anthu masiku ano amakonda kwambiri zinthu zina? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza kuti chikondi chenicheni n’chiyani ndipo tingakhale nacho bwanji.” Ŵerengani 1 Akorinto 13:2.

Galamukani! June 8

“Zikuoneka kuti masiku ano anthu ambiri amaganiza kuti makhalidwe abwino ndi opanda phindu kusiyana ndi mmene ankaganizira kale. Kodi nanunso mukuona choncho? [Yembekezani ayankhe.] Mochititsa chidwi, Baibulo linalosera izi. [Ŵerengani 2 Timoteo 3:1-5.] Magazini ya Galamukani! iyi ikufotokoza chifukwa chake makhalidwe a anthu akusintha ndiponso zimene zili m’tsogolo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena