Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/05 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
km 7/05 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda July 15

“Kwa zaka masauzande ambiri, anthu akhala ndi zikhulupiriro zosiyanasiyana. Kodi mukuganiza kuti n’zotheka kudziwa zikhulupiriro zimene zili zoona ndiponso zimene zili zabodza? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikutchula kumene mungapeze ziphunzitso zoona zimene Mulungu amakondwera nazo.” Werengani 2 Timoteo 3:16.

Galamukani! Aug. 8

“Zimapweteka mtima kwambiri kuona anthu akuvutika chifukwa cha masoka achilengedwe. [Tchulani chitsanzo chimene chikudziwika bwino kwanuko.] Kodi mukuganiza kuti masoka ngati amenewa akuwonjezereka? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikuyankha funso limeneli. Ilinso ndi mawu otonthoza kwa awo amene okondedwa awo anafa ndi masoka ngati amenewa.” Werengani Yohane 5:28, 29.

Nsanja ya Olonda Aug. 1

“Anthu ambiri masiku ano akuvutika maganizo podziona ngati anthu opanda pake. Kodi mukuganiza kuti pangafunike kuchitanji kuti tiwathandize? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza mmene Baibulo lingathandizire anthu oterowo kupeza chimwemwe chenicheni.” M’sonyezeni malemba akuda kwambiri olembedwa mopendekeka m’nkhani yakuti “Baibulo Lingakuthandizeni Kukhala Osangalala.”

Galamukani! Aug. 8

“Anthu ambiri akukhala mwamantha. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani anthu akukhala mwamantha chonchi? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ili ndi mfundo zothandiza kwambiri za mmene tingadzitetezere ku zinthu zofala zimene zimachititsa anthu kukhala mwamantha. Ikufotokozanso zimene Baibulo limalonjeza zoti dziko lidzakhala lopanda zoopsa.” Werengani Yesaya 11:9.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena