Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 7/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda July 15

“Anthu ambiri aona kuti anthu ochuluka ali ndi khalidwe losafuna kucheza ndi anzawo. Kodi mukuganiza kuti limeneli ndi khalidwe labwino? [Yembekezani ayankhe.] Taonani mawu anzeru awa onena za kufunika kocheza ndi ena. [Ŵerengani Mlaliki 4:9, 10.] Magazini iyi ikufotokoza chifukwa chimene tonsefe timafunira anzathu ndiponso mmene tingathetsere vuto losafuna kucheza ndi ena.”

Galamukani! July 8

“Anthu ambiri akusoŵa mtendere ndi kuchuluka kwa chiwawa chomwe ena amachita popanda cholinga chenicheni. [Tchulani chitsanzo chodziŵika kumeneko, ndipo yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikulongosola zinthu zina zimene zikuchititsa kuti pakhale chiwawa chankhanza chotere. Ikulongosolanso momwe Mulungu adzathetsere upandu ndi chiwawa moti sizidzakhalakonso.” Ŵerengani Salmo 37:10, 11.

Nsanja ya Olonda Aug. 1

“Kodi mukudziŵa kuti lipoti lina linati anthu oposa theka padziko lonse lapansi amagwiritsa ntchito ndalama zosakwana madola aŵiri patsiku? Kodi mukuganiza kuti pali china chilichonse chimene chingachitike kuti zimenezi zithe? [Yembekezani ayankhe.] Magazini ya Nsanja ya Olonda iyi ikutchula njira yopezeka m’Baibulo yothetseratu umphaŵi.”—Ŵerengani Salmo 72:12, 13, 16.

Galamukani! July 8

“Anthu ambiri akudera nkhaŵa chilengedwe. Kodi mukuganiza kuti zidzatheka kuteteza nkhalango za m’madera amene kumagwa mvula yambiri? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza zimene anthu akuchita masiku ano pofuna kuteteza nkhalango za m’madera amene kumagwa mvula yambiri. Ikufotokozanso momwe lonjezo labwino la Mulungu ili lidzakwaniritsidwire.” Ŵerengani Yesaya 11:9.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena