Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/04 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 7/04 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda July 15

“Ngati zochitika monga izi [zimene azisonyeza pa chikuto akanazilengeza pankhani lerolino, mwinamwake anthu ambiri sakanakhulupirira. Inu mukuganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Marko 4:39.] Kodi ndi umboni wotani umene umasonyeza kuti zozizwitsa zimene Yesu anazichita zinalidi zenizeni? Magazini iyi ya Nsanja ya Olonda ikuyankha funso limeneli.”

Galamukani! Aug. 8

“M’dzikoli, anthu ochita za chinyengo akuyesetsa kupeza njira zatsopano zobera anthu amene sakudziŵa chilichonse. Kodi zimenezi zikukukhudzani? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ya Galamukani! ikufotokoza zina mwa njira zofunika zimene zikhoza kutinthandiza kuti tidziteteze kwa anthu onyenga.” Ŵerengani Miyambo 22:3.

Nsanja ya Olonda Aug. 1

“Chifukwa cha kugaŵikana kwa anthu, ena amaganiza kuti njira yokha imene dziko lapansi lingakhalire pamtendere ndiyo kukhala ndi boma limodzi lolamulira padziko lonse lapansi. Kodi mukuganiza kuti zimenezi n’zotheka? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Danieli 2:44.] Magazini iyi ikunena zimene panopa Ufumu wa Mulungu ukuchita ndi mmene posachedwapa udzabweretsera dziko lamtendere.”

Galamukani! Aug. 8

“Tonsefe timamva chisoni tikamamva za mmene ana akuzunzidwira. Mwinamwake munadzifunsapo kuti, ‘Kodi Mulungu amawaganiziradi ana?’ [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Salmo 72:12-14.] Nkhani iyi ikufotokoza mmene Mulungu amaonera ana ndi mmene adzabweretsera mpumulo wachikhalire posachedwapa kwa onse amene akuzunzidwa.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena