Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/04 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 3/04 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Mar. 15

“Tikufuna kukuitanirani ku mwambo wa Mgonero wa Ambuye Lamlungu, pa April 4. [Fotokozani zimenezi pogwiritsa ntchito chikuto chakumapeto cha magaziniyi kapena timapepala toitanira anthu ku Chikumbutso. Ndiyeno ŵerengani Luka 22:19.] Nkhani zoyambirira m’magazini ya Nsanja ya Olonda iyi zikufotokoza tanthauzo la mwambo umenewu ndiponso mmene uyenera kuchitikira.”

Galamukani! Mar. 8

“Anthu ambiri amasangalala kuphunzira za nyama, ndipo ena amakonda kusunga nyama monga zoseŵera nazo. [M’loleni akambepo.] Magazini iyi ikufotokoza mavuto ena osunga nyama monga zoseŵera nazo. Ikufotokozanso za nthaŵi imene Mulungu walonjeza pamene nyama zonse zidzakhala mwamtendere ndipo zidzakhala pamtendere ndi anthu.” Ŵerengani Yesaya 11:6-9.

Nsanja ya Olonda Apr. 1

“Ndi nkhani zochepa chabe m’Baibulo zimene zapatsa anthu maganizo kwambiri ngati mmene yachitira nkhani yovuta kuimvetsa yofotokoza chizindikiro cha chirombo. Kodi munaimvapo nkhani imeneyi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Chivumbulutso 13:16-18.] M’Baibulo momwemo mumapezeka mfundo zimene zingathandize kumvetsa tanthauzo la nkhani yovuta imeneyi. Magazini iyi ikufotokoza mfundozo.”

Galamukani! Mar. 8

“M’mbuyomu, anthu ambiri anali kuopa nkhondo ya zida za nyukiliya. Kodi mukuganiza kuti nkhondo ya zida zimenezi ingakhaleko masiku ano? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza zinthu zodetsa nkhaŵa zimene zikuchitika panopa. Ikufotokozanso zimene Baibulo lalonjeza kuti kudzakhala dziko lopanda mantha.” Ŵerengani Zefaniya 3:13.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena