Zofunika Kukumbukira pa Chikumbutso
Chikumbutso cha chaka chino chidzachitika Lachitatu, pa April 12. Akulu akumbukire zinthu izi:
◼ Pokonza nthawi ya mwambowu, onetsetsani kuti musapereke zizindikiro dzuwa lisanalowe.
◼ Aliyense, ngakhale wokamba nkhani, auzidwe nthawi yeniyeni ndi kumene kudzachitikire mwambowu.
◼ Mupezeretu mkate ndi vinyo woyenera.—Onani Nsanja ya Olonda ya February 15, 2003, tsamba 14 ndi 15.
◼ Mbale, matambula, tebulo labwino ndi nsalu za patebulo ziyenera kubwera ku holo nthawi yabwino n’kuziikiratu pamalo ake.
◼ Nyumba ya Ufumu kapena malo ena alionse ochitirapo mwambowu akonzedweretu bwinobwino.
◼ Muyenera kusankhiratu akalinde ndi operekera zizindikiro ndipo muwauziretu ntchito yawo ndi mmene adzayendetsere zinthu, ndiponso kuti afunika adzavale zovala zaulemu ndiponso kudzikonza bwino.
◼ Konzani zokapereka zizindikirozo kwa wodzozedwa aliyense amene akudwala ndipo satha kupezekapo.
◼ Ngati mipingo ingapo idzagwiritsa ntchito Nyumba ya Ufumu imodzi, mipingoyo iyenera kugwirizana bwino, kuti anthu asadzapanikizane pakhonde, pakhomo, m’tinjira, ndi koimika magalimoto.