Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/09 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
km 9/09 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda September 1

“Anthu ambiri amaganiza kuti nkhani ya Adamu ndi Hava ya m’buku la Genesis ndi yongopeka. Koma ena amakhulupirira kuti Adamu ndi Hava anali anthu enieni. Kodi inuyo mukuganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Yesu ananena. [Werengani Maliko 10:6-9.] Nkhaniyi ikuunika umboni wokhudza nkhani imeneyi ndipo ikusonyeza kuti zimene timakhulupirira pankhaniyi n’zofunika kwambiri.” Sonyezani nkhani imene yayambira patsamba 12.

Galamukani! September

Werengani 1 Yohane 4:8. Ndiyeno nenani kuti: “Anthu ena amakhulupirira kuti Mulungu amalanga ndi moto anthu oipa. Ena amaona kuti maganizo amenewa sagwirizana ndi zimene tawerengazi. Kodi inuyo mukuganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe.] Nkhaniyi ikufotokoza zimene Baibulo limaphunzitsa.” Sonyezani nkhani yomwe yayambira patsamba 10.

Nsanja ya Olonda October 1

“Tonsefe timakumana ndi mavuto. [Tchulani ena mwa mavuto amene anthu amakumana nawo m’gawo lanu.] Kodi mukuganiza kuti Mulungu angatithandize kuthetsa mavuto amenewa? [Yembekezani ayankhe.] Pavesi ili Yesu anatchula njira imodzi imene Mulungu amatithandizira. [Werengani Luka 11:13.] Magaziniyi ikuthandizani kudziwa kuti mzimu woyera n’chiyani komanso kudziwa mmene ungakuthandizireni.”

Galamukani! October

“Banja lililonse limakumana ndi mavuto. Kodi mukuganiza kuti mabanja angapeze kuti malangizo odalirika? [Yembekezani ayankhe. Kenako werengani Salmo 32:8.] Galamukani! iyi ndi yapadera ndipo ikufotokoza mfundo zingapo za m’Baibulo zimene zingathandize kwambiri mabanja.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena