Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/10 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
km 9/10 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda September 1

“Nthawi zina anthu amachita zinthu zoipa chifukwa chotengeka ndi zinthu zonyenga zimene chipembedzo chawo chimaphunzitsa. Kodi mukuganiza kuti n’chiyani chimawachititsa kuti azinyengedwe kwambiri choncho? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo limanena. [Werengani 1 Yohane 4:1.] Magazini iyi ikufotokoza kufunika koyerekezera zimene timakhulupirira ndi zimene Mawu a Mulungu amanena.” Kenako, muonetseni nkhani imene ikuyambira patsamba 10.

Galamukani! September

Werengani Mateyo 5:39. Kenako, funsani kuti: “Kodi mukuganiza kuti Yesu ankatanthauza kuti tiyenera kungoyang’ana ena akamatichitira zoipa? [Yembekezani ayankhe.] Nkhani iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena pa nkhani yodziteteza ndiponso yokadandaula kukhoti.” Kenako muonetseni nkhani imene ikuyambira patsamba 10.

Nsanja ya Olonda October 1

“Anthu azipembedzo zosiyanasiyana amapemphera. Kodi mukuganiza kuti Mulungu amamvetseradi ndi kuyankha mapemphero? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limatilimbikitsa kupemphera. [Werengani Afilipi 4:6, 7.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena pa mafunso 7 okhudza pemphero amene anthu ambiri amafunsa.”

Galamukani! October

“Nthawi zambiri timamva za anthu amene amachitidwa zachinyengo ndi amuna kapena akazi awo, anthu andale, ndiponso anthu ena. Kodi mukuganiza kuti kupeza anthu oti mungawakhulupirire n’kovuta? [Yembekezani ayankhe.] Anthu ambiri amaona kuti lemba ili likukwaniritsidwa. [Werengani 2 Timoteyo 3:1-5.] Magazini iyi ikufotokoza kumene mungapezebe anthu okhulupirika.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena