Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/09 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
km 10/09 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda October 1

“Masiku ano anthu ambiri asiya kukhulupirira zoti pali Mlengi. Kodi mukuganiza kuti akuchita zimenezi chifukwa chiyani? [Yembekezani ayankhe. ] Chifukwa china chikupezeka pa mavesi awa. [Werengani Habakuku 1:2, 3.] Nkhani iyi ikuthandizani kuyankha mafunso okhudza Mulungu amene achititsa anthu ena kusiya kum’khulupirira.” Asonyezeni nkhani imene yayambira patsamba 11.

Galamukani! October

“Kodi n’zoona kuti mabanja akukumana ndi mavuto ambiri masiku ano? [Yembekezani ayankhe.] Anthu ambiri samadziwa malangizo othandiza amene ali m’Baibulo. Mwachitsanzo, taonani malangizo awa.” [Werengani lemba lililonse lopezeka m’magaziniyi.] Galamukani! yapadera imeneyi ikusonyeza mmene mfundo za m’Baibulo zingathandizire mabanja kuthetsa mavuto osiyanasiyana.”

Nsanja ya Olonda November 1

“Kodi mukuganiza kuti zonse zimene amaphunzitsa m’matchalitchimu zimachokera m’Baibulo? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limatichenjeza kuti tikhale osamala ndi ziphunzitso zonama. [Werengani Akolose 2:8.] Magazini iyi ikufotokoza ziphunzitso 6 zosagwirizana ndi Mawu a Mulungu zimene amaphunzitsa m’matchalitchi osiyanasiyana.”

Galamukani! November

“Masiku ano anthu ambiri akugwiritsa ntchito zipangizo zamakono monga mafoni am’manja ndi makompyuta. Kodi mukuganiza kuti kugwiritsa ntchito zipangizo zamakono kumatithandiza kuchita zinthu mwamsanga kapena kumatithera nthawi? [Yembekezani ayankhe.] Anthu ambiri angagwirizane ndi malangizo awa olimbikitsa kugwiritsa ntchito nthawi mwanzeru. [Werengani Aefeso 5:15, 16.] Magazini iyi ikufotokoza mfundo zimene tingatsatire kuti tizigwiritsa ntchito zipangizo zamakono moyenerera.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena