Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/11 tsamba 7
  • Kodi Likuoneka Bwanji?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Likuoneka Bwanji?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mumayamikira Mabuku Athu?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Gwiritsani Ntchito Mwanzeru Mabuku Athu Ofotokoza Baibulo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Bokosi La Mafunso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Bokosi la Mafunso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
km 10/11 tsamba 7

Kodi Likuoneka Bwanji?

Limeneli ndi funso labwino kwambiri kudzifunsa tikamafuna kugawira buku lililonse? Buku lililonse limene layamba kupindika m’makona, kuchoka mtundu wake, kuda kapena kung’ambika silipereka chithunzi chabwino cha gulu lathu ndipo likhoza kulepheretsa mwininyumba kumva uthenga wabwino ndiponso wopulumutsa moyo womwe uli m’mabukuwo.

Kodi tingatani kuti mabuku athu azikhala ooneka bwino? Anthu ambiri amaona kuti n’zothandiza kukonza zoti m’chikwama chawo cha mu utumiki, mabuku a mtundu umodzi azikhala pamodzi. Mwachitsanzo, amakhala ndi malo a mabuku, magazini, mabulosha ndipo mbali ina mathirakiti ndi zina zotero. Akamabwezera Baibulo ndi mabuku ena onse pamalo ake, amawaika mosamala kwambiri kuti asaonongeke. Ofalitsa ena amaika mabuku awo mu zinthu zina kapena m’mapepala a pulasitiki. Kaya tikusunga mabuku athu motani, tiyeni tiyesetse kupewa kugawira munthu mabuku owonongeka chifukwa zimenezi zingamupatse chifukwa chomveka chokanira uthenga wathu.—2 Akor. 6:3.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena