Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/12 tsamba 8
  • Zitsanzo za Ulaliki

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zitsanzo za Ulaliki
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Nkhani Yofanana
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
km 6/12 tsamba 8

Zitsanzo za Ulaliki

Zimene Munganene Poyambitsa Maphunziro a Baibulo Loweruka Loyambirira M’mwezi wa July

“M’zaka zaposachedwapa, anthu akhala akukamba kwambiri nkhani za angelo. Kodi mukuganiza kuti angelo ndi enieni? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene magazini iyi ikunena pa nkhaniyi.” M’patseni Nsanja ya Olonda ya July 1 ndipo mukambirane naye mfundo zimene zili pa kamutu koyamba patsamba  16. Komanso muwerenge lemba ngakhale limodzi lokha pa malemba amene akupezeka pa kamutu koyambaka. Mugawireni magaziniyo n’kupangana naye tsiku limene mudzayankhe funso lotsatira.

Nsanja ya Olonda July 1

Werengani Salimo 65:2. Kenako munene kuti: “Anthu ambiri amavomereza kuti Mulungu ndi ‘Wakumva pemphero,’ ndipo amapemphera tsiku lililonse. Koma anthu ena amadabwa kuti, ‘Ngati kuli Mulungu, n’chifukwa chiyani dziko lapansili lili ndi mavuto ambirimbiri chonchi?’ Inu mukuganiza bwanji? Kodi Mulungu amamvadi mapemphero athu? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena poyankha funso lakuti: ‘N’chifukwa chiyani Mulungu amene amamva mapemphero athu amalola kuti tizivutika?’”

Galamukani! July

“Ngati mutapatsidwa mwayi woti musinthe zinazake padzikoli, kodi mungasinthe chiyani? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limafotokoza chimene chimachititsa kuti tizilephera kukwaniritsa zimene timafuna. [Werengani Yeremiya 10:23.] Magazini iyi ikufotokoza zinthu zimene Mulungu akufuna kusintha.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena