Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/11 tsamba 8
  • Zitsanzo za Ulaliki

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zitsanzo za Ulaliki
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kuti Muyambitse Maphunziro a Baibulo Loweruka Loyambirira M’mwezi wa May
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
km 4/11 tsamba 8

Zitsanzo za Ulaliki

Kuti Muyambitse Maphunziro a Baibulo Loweruka Loyambirira M’mwezi wa May

“Kodi munadzifunsapo kuti n’chifukwa chiyani Mulungu amalola kuti zoipa zizichitika ndiponso kuti anthu azivutika? [Yembekezani ayankhe.] Ndikufuna ndikusonyezeni mfundo yosangalatsa pa nkhani imeneyi.” Kenako werengani limodzi zimene zili pakamutu koyamba patsamba 16 mu Nsanja ya Olonda ya May 1 ndiponso lemba limodzi limene laikidwa pamenepo. Mukatero apatseni magaziniyo ndipo mupangane zoti mudzabwerenso kuti mudzakambirane yankho la funso lotsatiralo.

Nsanja ya Olonda May 1

Werengani Salimo 37:10, 11. Ndiye funsani kuti: “Kodi mukuganiza kuti lonjezo limeneli likwaniritsidwa posachedwapa? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza maulosi 6 a m’Baibulo amene akukwaniritsidwa panopo. Maulosi amenewa akusonyeza kuti lonjezo tawerengali latsala pang’ono kukwaniritsidwa.”

Galamukani! May

“Anthu ena amanena kuti anthufe tinachokera ku nyama. Inu mumaganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe. Kenako werengani Salimo 139:14.] Wolemba Masalimoyu sankadziwa zinthu zambiri zodabwitsa zokhudza thupi la munthu ayi. Magazini iyi ikufotokoza zimene zikudziwika panopo ndiponso zimene zimatisiyanitsa ndi nyama.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena