Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 July tsamba 1
  • Zitsanzo za Ulaliki

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zitsanzo za Ulaliki
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • NSANJA YA OLONDA
  • NSANJA YA OLONDA (tsamba lomaliza)
  • UTHENGA WABWINO WOCHOKERA KWA MULUNGU
  • LEMBANI ULALIKI WANUWANU
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 July tsamba 1
Wofalitsa akulalikira munthu wothyola tiyi ku Cameroon

Akulalikira munthu wothyola tiyi ku Cameroon

Zitsanzo za Ulaliki

NSANJA YA OLONDA

Nsanja ya Olonda, Na. 4 | Baibulo Lapulumuka M’zinthu Zambiri

Funso: Kwa zaka zambiri, anthu ena akhala akuchita zinthu zosiyanasiyana kuti Baibulo lisapezekenso, koma mpaka pano lidakalipobe. Kodi umenewu si umboni wokwanira woti linachokeradi kwa Mulungu?

Lemba: Yes. 40:8

Perekani Magaziniyo: Nkhani zomwe zili m’magaziniyi zikufotokoza zimene anthu akhala akuchita pofuna kuti Baibulo lisapezekenso.

NSANJA YA OLONDA (tsamba lomaliza)

Funso: Ndikufuna kumva maganizo anu pa funso ili. [Werengani funso loyamba patsamba 16.] Anthu ena amakhulupirira kuti anthu ndi amene anayambitsa zipembedzo. Koma ena amaganiza kuti Mulungu ndi amene anayambitsa chipembedzo kuti anthu azimulambira. Kodi inuyo mukuganiza bwanji?

Lemba: Yak. 1:27

Perekani Magaziniyo: Nkhaniyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena pa nkhani imeneyi. Ndidzabweranso kuti tidzakambirane mfundo zina za m’nkhaniyi.

UTHENGA WABWINO WOCHOKERA KWA MULUNGU

Uthenga Wabwino Wochokera kwa Mulungu

Funso: Nkhani zimene anthu amawerenga m’nyuzipepala masiku ano ndi zimene Baibulo linaneneratu. Kodi ndi zinthu ziti zimene Baibulo linaneneratu zomwe inuyo munamva kapena kuona zikuchitika?

Lemba: 2 Tim. 3:1-5

Perekani Kabukuko: Kabukuka kakufotokoza kuti anthu amene amakonda Mulungu amaona kuti zikuchitikazi ndi chizindikiro choti tili m’masiku otsiriza. [Muonetseni funso lachiwiri pamutu woyamba.]

LEMBANI ULALIKI WANUWANU

Potengera zitsanzozi, konzani njira imene mungagwiritse ntchito.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena