Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 March tsamba 5
  • Kodi Tingagwiritse Ntchito Bwanji Kabuku Kakuti Mverani Mulungu?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Tingagwiritse Ntchito Bwanji Kabuku Kakuti Mverani Mulungu?
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Thandizani Anthu Kumvera Mulungu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Gwiritsani Ntchito Kabuku Kakuti Uthenga Wabwino Wochokera kwa Mulungu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Chiŵiya Chatsopano Chothandiza Nacho Anthu Kuphunzira Zimene Mulungu Amafuna
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Muzigwiritsa Ntchito Kabuku Ndi Buku Lakuti “Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale” mu Utumiki
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 March tsamba 5

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Kodi Tingagwiritse Ntchito Bwanji Kabuku Kakuti Mverani Mulungu?

Mverani Mulungu

Kabuku kakuti Mverani Mulungu kanapangidwa n’cholinga choti tizigwiritsa ntchito pophunzira ndi anthu amene amavutika kwambiri kuwerenga. Kamatithandiza kuphunzitsa mfundo zikuluzikulu za m’Baibulo pogwiritsa ntchito zithunzi. Phunziro lililonse ndi la masamba awiri ndipo lili ndi zithunzi zokonzedwa bwino zomwe zili ndi mivi yolozera chithunzi chotsatira.

Kabuku kakuti Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha kali ndi zithunzi zofanana ndi za m’kabuku kakuti Mverani Mulungu koma kali ndi mawu ambiriko ndipo tikhoza kukagwiritsa ntchito pophunzira ndi anthu amene savutika kwambiri kuwerenga. Ofalitsa ambiri amakonda kugwiritsa ntchito kabukuka akamaphunzira ndi anthu kabuku kakuti Mverani Mulungu. Masamba ambiri ali ndi kabokosi kamene kali ndi mfundo zowonjezera zomwe tingakambirane ndi wophunzira wathu ngati tikuona kuti angazimvetse.

Mlongo akugwiritsa ntchito kabuku ka Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha pomwe wophunzira wake akugwiritsa ntchito kabuku ka Mverani Mulungu

Mukhoza kugawira timabukuti mwezi uliwonse. Mukamaphunzira timabukuti ndi anthu, muzigwiritsa ntchito zithunzi powafotokozera nkhani za m’Baibulo. Muzifunsa mafunso kuti wophunzira azinena maganizo ake komanso kuti mudziwe ngati akumvetsa zimene akuphunzirazo. Muziwerenga ndiponso kukambirana malemba amene ali m’munsi mwa tsamba lililonse. Mukamaliza kabukuka, mungayambe kuphunzira naye buku lakuti Zimene Baibulo Limaphunzitsa kuti mumuthandize kudziwa zambiri ndiponso kubatizidwa.

Phunziro la m’kabuku ka Mverani Mulungu lofotokoza za Adamu ndi Hava ali m’munda wa Edeni
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena