Akugawira kapepala kakuti Akufa Adzauka? ku Tuvalu
Zitsanzo za Ulaliki
GALAMUKANI!
Funso: N’chifukwa chiyani tiyenera kukonzekera ngozi zadzidzidzi?
Lemba: Miy. 27:12
Perekani Magaziniyo: Magazini iyi ikufotokoza zimene tingachite ngozi isanachitike, ikamachitika komanso pambuyo poti yachitika.
KUPHUNZITSA CHOONADI
Funso: Kodi timasonyeza bwanji kuti timakonda Mulungu?
Lemba: 1 Yoh. 5:3
Zoona Zake: Timasonyeza kuti timakonda Mulungu tikamamvera malamulo ake.
KODI N’ZOONADI KUTI AKUFA ADZAUKA? (T-35)
Funso: Chaka chilichonse, anthu ambiri padziko lonse amachita miyambo yolemekeza akufa. Kodi n’zotheka kudzaonananso ndi achibale komanso anzathu amene anamwalira?
Lemba: Mac. 24:15
Perekani Kapepalako: Kapepala aka kakufotokoza mmene chiyembekezo choti akufa adzauka chingatithandizire. [Ngati n’kotheka, muonetseni vidiyo yakuti Kodi Anthu Amene Anamwalira Adzakhalanso ndi Moyo?]
LEMBANI ULALIKI WANUWANU
Potengera zitsanzozi, konzani njira imene mungagwiritse ntchito