Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 February tsamba 3
  • Tingaphunzire Chiyani Kuchokera mu Nyimbo za Broadcasting?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tingaphunzire Chiyani Kuchokera mu Nyimbo za Broadcasting?
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Nyimbo Zomwe Zimatithandiza Kuyandikira Mulungu
    Kodi Zopereka Zanu Zimagwiritsidwa Ntchito Bwanji?
  • Tizitamanda Yehova Mosangalala Poimba Nyimbo
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nyimbo za Ufumu Zimatithandiza Kukhala Olimba Mtima
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Mfundo Zothandiza Pophunzira
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 February tsamba 3
Abale ndi alongo akuimba nyimbo pogwiritsa ntchito gitala.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Kodi Tingaphunzire Chiyani Kuchokera mu Nyimbo za Broadcasting?

Kodi pa nyimbo zomwe zimatuluka pa JW Broadcasting, ndi nyimbo iti imene mumaikonda kwambiri, nanga n’chifukwa chiyani? Kodi mumaona kuti zimene zimasonyezedwa m’mavidiyo a nyimbozi ndi zofanana ndi zimene zimakuchitikirani? Aliyense akhoza kusangalala ndi nyimbozi chifukwa zili ndi mitu yosiyanasiyana komanso zimaimbidwa m’zamba zambiri. Komabe sikuti nyimbozi komanso mavidiyo ake zimakonzedwa n’cholinga choti zizingotisangalatsa basi.

Nyimbo iliyonse ili ndi mfundo zothandiza zimene tingazigwiritse ntchito pa moyo wathu komanso mu utumiki. Nyimbo zina zimanena za kuchereza alendo, mgwirizano, mabwenzi, kulimba mtima, chikondi komanso chikhulupiriro. Zinanso zimakhala ndi uthenga wothandiza munthu kubwerera kwa Yehova, kukhululukira ena, kukhalabe okhulupirika kwa Yehova komanso kukhala ndi zolinga zauzimu. Palinso nyimbo ina yomwe imatithandiza kuona kufunika kogwiritsa ntchito bwino mafoni athu. Kodi ndi mfundo zina ziti zothandiza zimene mwapeza m’nyimbo zathu?

ONERANI VIDIYO YA NYIMBO YAKUTI DZIKO LATSOPANO LILI PAFUPI, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi m’vidiyoyi, m’bale ndi mlongo wachikulireyu akuganizira za madalitso ati a m’tsogolo?​—Gen. 12:3

  • Kodi tingalimbitse bwanji chikhulupiriro chathu choti Yehova amakwaniritsa malonjezo ake?

  • Kodi tikuyembekezera chiyani m’tsogolomu?

  • Kodi zimene tikuyembekezera kutsogoloku zimatithandiza bwanji kupirira mavuto amene tikukumana nawo?​—Aroma 8:25

YESANI KUCHITA IZI PA KULAMBIRA KWANU KWA PABANJA

Onerani mavidiyo a nyimbo zotsatirazi, kenako yankhani mafunso awiriwa: Kodi ndi mfundo zothandiza ziti zimene ndikuphunzira m’mavidiyowa? Nanga ndingazigwiritse ntchito bwanji pa moyo wanga?

  • Tisaope

  • Tizikhululukirana

  • “Khalani Ochereza”

  • Tiyendebe

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena