Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w23 November tsamba 32
  • Mfundo Zothandiza Pophunzira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mfundo Zothandiza Pophunzira
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Muziloweza “Nyimbo Zauzimu”
  • Tizitamanda Yehova Mosangalala Poimba Nyimbo
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Kodi Mwakonzekera Kuimbira Yehova Pamisonkhano?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Nyimbo Zatsopano
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Nyimbo Zomwe Zimatithandiza Kuyandikira Mulungu
    Kodi Zopereka Zanu Zimagwiritsidwa Ntchito Bwanji?
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
w23 November tsamba 32

Mfundo Zothandiza Pophunzira

Muziloweza “Nyimbo Zauzimu”

Lorraine wa ku U.S.A. ananena kuti, “Ndikayamba kudziona ngati wachabechabe, Yehova amandilimbikitsa pogwiritsa ntchito nyimbo za pa JW Broadcasting®.”

Akhristu akhala akugwiritsa ntchito “nyimbo zauzimu” polambira. (Akol. 3:16) Ngati mutaphunzira komanso kuloweza nyimbozi zingakuthandizeni ngakhale pamene mulibe buku kapena chipangizo chamakono. Mfundo zotsatirazi zingakuthandizeni kuti muzitha kuloweza nyimbozi.

  • Muziwerenga mawu ake mosamala kuti mumvetse tanthauzo lake. Munthu amatha kukumbukira mawu ngati wamvetsa tanthauzo lake. Pa jw.org pamapezeka mawu a nyimbo zathu kuphatikizapo za Broadcasting komanso za ana. Pitani pamene alemba kuti Laibulale, kenako Nyimbo.

  • Muzilemba mawu a nyimboyo pamanja. Mukamachita zimenezo m’pamene mawu a nyimboyo amakhazikika m’maganizo mwanu.—Deut. 17:18.

  • Muziyeserera motulutsa mawu. Muziwerenga komanso kuimba mawu a nyimboyo mobwerezabwereza.

  • Dziyeseni kuti muone ngati mwaloweza. Muziyesa kukumbukira mawu a nyimboyo popanda kuonera, kenako muziona ngati mwawaloweza.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena